Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 45 tsamba 110-tsamba 111 ndime 2
  • Ufumu Unagawikana

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ufumu Unagawikana
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Ufumu Ukugawanika
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Yehova Sataya Anthu Ake Okhulupirika
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Akanatha Kusangalatsa Mulungu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Mafumu Woyamba
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 45 tsamba 110-tsamba 111 ndime 2
Ahiya akung’amba chovala chake zidutswa zokwana 12 Yerobowamu akuona

MUTU 45

Ufumu Unagawikana

Pamene Solomo ankalambira Yehova, ku Isiraeli kunali mtendere. Koma kenako anakwatira akazi ambiri a mitundu ina ndipo akaziwa ankalambira mafano. Pang’ono ndi pang’ono, Solomo anasintha ndipo nayenso anayamba kulambira mafano. Yehova anakwiya kwambiri ndi zimenezi. Ndiyeno anauza Solomo kuti: ‘Ufumu wa Isiraeli uchotsedwa ku banja lako ndipo ugawikana pawiri. Ndidzapereka mbali yaikulu ya ufumuwu kwa mtumiki wako ndipo banja lako lidzatsala ndi mbali yochepa.’

Yehova anachitanso zinthu zina posonyeza kuti zimenezi zidzachitikadi. Tsiku lina, mtumiki wina wa Solomo dzina lake Yerobowamu anali pa ulendo ndipo anakumana ndi mneneri Ahiya. Ahiya anang’amba chovala chake zidutswa zokwana 12. Atatero anauza Yerobowamu kuti: ‘Yehova achotsa ufumu wa Isiraeli ku banja la Solomo ndipo augawa pawiri. Tenga zidutswa 10 izi chifukwa iweyo udzakhala mfumu ya mafuko 10.’ Mfumu Solomo atamva zimenezi, ankafuna kupha Yerobowamu. Choncho Yerobowamu anathawira ku Iguputo. Patapita nthawi, Solomo anamwalira ndipo mwana wake Rehobowamu anakhala mfumu. Zitatero Yerobowamu anaona kuti akhoza kubwerera ku Isiraeli.

Aisiraeli ambiri akupereka nsembe kwa fano la mwana wa ng’ombe amene Yerobowamu waimika

Akuluakulu a ku Isiraeli anauza Rehobowamu kuti: ‘Mukamawalamulira bwino anthuwa, akhala okhulupirika kwa inu.’ Koma achinyamata anzake anamuuza kuti: ‘Anthuwa musamawalamulire mowanyengerera. Muziwagwiritsa ntchito zolemetsa kuposa zimene bambo anu ankawagwiritsa.’ Rehobowamu anamvera malangizo amenewa. Choncho ankalamulira anthuwo mwankhanza ndipo iwo anamuukira. Anthuwo anasankha Yerobowamu kuti akhale mfumu ya mafuko 10, omwe ankadziwika kuti ufumu wa Isiraeli. Mafuko awiri okha ndi amene anakhalabe okhulupirika kwa Rehobowamu ndipo ankadziwika kuti ufumu wa Yuda. Apa ndiye kuti mafuko 12 a Aisiraeli anagawikana.

Yerobowamu sankafuna kuti anthu ake azipita kukalambira ku Yerusalemu kumene mfumu yake anali Rehobowamu. Kodi ukudziwa chifukwa chake? Yerobowamu ankaopa kuti anthuwo akhoza kumuukira n’kupita kumbali ya Rehobowamu. Choncho anapanga mafano awiri a ana a ng’ombe n’kuuza anthuwo kuti: ‘Muzilambirira konkuno, chifukwatu ku Yerusalemu n’kutali.’ Ndiye anthuwo anayambadi kulambira ana a ng’ombewo ndipo anaiwala Yehova.

“Musamangidwe mʼgoli ndi osakhulupirira, chifukwa ndinu osiyana. Pali mgwirizano wotani pakati pa chilungamo ndi kusamvera malamulo?  . . . Nanga munthu wokhulupirira ndi wosakhulupirira angafanane pa zinthu ziti?”—2 Akorinto 6:14, 15

Mafunso: N’chifukwa chiyani ufumu wa Isiraeli unagawikana? Kodi Mfumu Rehobowamu komanso Mfumu Yerobowamu anachita zoipa zotani?

1 Mafumu 11:1-13, 26-43; 12:1-33

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena