Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 46 tsamba 112-tsamba 113 ndime 1
  • Zimene Zinachitika Paphiri la Karimeli

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Zinachitika Paphiri la Karimeli
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Sanasunthike pa Kulambira Koona
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
  • Sanasunthike Pakulambira Koona
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Eliya Atamanda Mulungu Woona
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Anali Watcheru Ndiponso Anadikira
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 46 tsamba 112-tsamba 113 ndime 1
Moto wochokera kwa Yehova ukupsereza nsembe ya Eliya

MUTU 46

Zimene Zinachitika Paphiri la Karimeli

Ufumu wa mafuko 10 wa Isiraeli unali ndi mafumu ambiri oipa. Koma Mfumu Ahabu ndi amene anali woipa kuposa onsewo. Iye anakwatira mkazi woipa amene ankalambira Baala ndipo dzina lake anali Yezebeli. Ahabu ndi Yezebeli ankapha aneneri a Yehova komanso anapangitsa kuti anthu ambiri a ku Isiraeli azilambira Baala. Ndiye kodi Yehova anatani? Anatumiza mneneri Eliya kuti akapereke uthenga kwa Ahabu.

Eliya anauza mfumuyi kuti popeza inkachita zoipa, m’dziko la Isiraeli simugwa mvula. Kwa zaka zoposa zitatu anthu sanathe kulima chakudya chifukwa kunali chilala. Choncho m’dzikolo munagwa njala. Kenako Yehova anatumizanso Eliya kwa Ahabu. Ndiyeno mfumuyo inati: ‘Iwe ndi amene wabweretsa mavuto onsewa.’ Koma Eliya anayankha kuti: ‘Ayi si ine. Mwabweretsa chilalachi ndi inuyo chifukwa mukulambira Baala. Sonkhanitsani anthu ndi aneneri a Baala pamwamba pa phiri la Karimeli kuti tikaone umboni wa zimenezi.’

Anthu anasonkhanadi paphirilo. Ndiyeno Eliya anawauza kuti: ‘Sankhani Mulungu woti muzimulambira. Ngati Yehova ali Mulungu woona mʼtsatireni, koma ngati Mulungu woona ndi Baala tsatirani ameneyo. Atumiki 450 a Baala akonze nsembe ndipo apemphere kwa mulungu wawo kuti apsereze nsembeyo. Inenso ndikonza nsembe yanga ndipo ndipemphera kwa Yehova kuti aipsereze. Mulungu amene angathe kupserezadi nsembezi ndiye woona.’ Anthuwo anavomera.

Aneneri a Baala anakonzadi nsembe yawo. Iwo anapemphera kwa mulungu wawo tsiku lonse kuti: ‘Inu a Baala, tiyankheni!’ Koma Baala sanawayankhe. Kenako Eliya anayamba kuwaseka. Anawauza kuti: ‘Muitaneni mokweza. Mwina wagona ndipo pakufunika wina amudzutse.’ Aneneri a Baala anapitirizabe kupemphera mpaka madzulo koma Baalayo sanawayankhe.

Kenako Eliya anaika nsembe yake paguwa ndipo anathirapo madzi. Ndiyeno anapemphera kuti: ‘Inu Yehova, chititsani kuti anthu awa adziwe kuti inu ndinu Mulungu woona.’ Nthawi yomweyo Yehova anatumiza moto kuchokera kumwamba ndipo unapsereza nsembeyo. Anthu ataona zimenezi anayamba kufuula kuti: “Mulungu woona ndi Yehova!” Eliya anati: “Gwirani aneneri a Baala! Muonetsetse kuti pasapezeke wothawa!” Pa tsikuli aneneri onse a Baala okwana 450 anawapha.

Kenako kunyanja kunaoneka kamtambo kakang’ono ndipo Eliya anauza Ahabu kuti: ‘Kugwa chimvula champhamvu. Kwerani galeta muzipita kwanu.’ Mwadzidzidzi kunja kunachita mdima wa mitambo, kunayamba kuwomba chimphepo ndipo kenako chimvula chinayamba kugwa. Apa ndiye kuti chilala chija chinatha. Ahabu anayamba kuthamangitsa galeta lake n’cholinga choti chimvulacho chisamutsekereze. Koma mothandizidwa ndi Yehova, Eliya anathamanga mpaka kupitirira galeta la Ahabu lija. Ndiye kodi mavuto a Eliya anathera pamenepa? Tiona m’nkhani yotsatira.

“Anthu adziwe kuti inu, amene dzina lanu ndinu Yehova, inu nokha ndinu Wamʼmwambamwamba, woyenera kulamulira dziko lonse lapansi.”​—Salimo 83:18

Mafunso: Kodi paphiri la Karimeli panachitika zotani? Kodi Yehova anayankha bwanji pemphero la Eliya?

1 Mafumu 16:29-33; 17:1; 18:1, 2, 17-46; Yakobo 5:16-18

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena