Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 48 tsamba 116-tsamba 117 ndime 1
  • Mwana wa Mayi Wamasiye Anaukitsidwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mwana wa Mayi Wamasiye Anaukitsidwa
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mkazi Wamasiye wa ku Zarefati Anadalitsidwa Chifukwa cha Chikhulupiriro
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Kodi Muli ndi Chikhulupiriro Chonga cha Eliya?
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Analimbikitsidwa ndi Mulungu Wake
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
  • Analimbikitsidwa Ndi Mulungu Wake
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 48 tsamba 116-tsamba 117 ndime 1
Eliya akuitana mayi wamasiye amene akutola nkhuni

MUTU 48

Mwana wa Mayi Wamasiye Anaukitsidwa

Mtsuko wa ufa ndi wa mafuta

Pamene ku Isiraeli kunali chilala, Yehova anauza Eliya kuti: ‘Pita ku Zarefati. Kumeneko mayi wina wamasiye azikakupatsa chakudya.’ Eliya atafika mumzindawo, anaona mayi wosauka komanso wamasiye akutola nkhuni. Iye anam’pempha kuti amupatseko madzi. Pamene mayiyo ankapita kukatenga madziwo, Eliya anamuuzanso kuti: ‘Mundibweretserekonso chakudya pang’ono.’ Koma mayiyo anati: ‘Ndilibe chakudya choti ndingakupatseni. Ndangotsala ndi kaufa kochepa ndi timafuta toti ndiphikire chakudya chokwanira ineyo ndi mwana wanga basi.’ Koma Eliya anamuuza kuti: ‘Yehova wanena kuti mukandipatsa, ndiye kuti ufa ndi mafuta anu sizitha mpaka mvula idzagwe.’

Ndiyeno mayiyo anapita kukakonza chakudya n’kupatsa mneneri wa Yehovayo. Mogwirizana ndi zimene Yehova ananena, mayiyo ndi mwana wake anali ndi chakudya pa nthawi yonse yachilalayo. Mtsuko wake wa ufa komanso wa mafuta unkangokhalabe wodzadza.

Kenako panachitika zinthu zomvetsa chisoni. Mwana uja anadwala kwambiri mpaka kumwalira. Ndiyeno mayiyo anapempha Eliya kuti amuthandize. Eliya anatenga mwana wakufayo n’kupita naye kuchipinda cham’mwamba. Anamugoneka pabedi ndipo anapemphera kuti: ‘Chonde Yehova, ukitsani mwanayu.’ Kodi ukuganiza kuti n’chifukwa chiyani zimene Eliya anapemphazi zinali zodabwitsa? Chifukwa kuyambira kalekale, zimenezi zinali zisanachitikepo. Komanso mayiyu ndi mwana wakeyo sanali Aisiraeli.

Koma mwana uja anakhalanso ndi moyo ndipo anayamba kupuma. Eliya anauza mayiyo kuti: ‘Mwana wanu uja tsopano ali moyo.’ Mayiyo anasangalala kwambiri ndipo anauza Eliya kuti: ‘Ndinudi munthu wa Mulungu. Ndikutero chifukwa mumalankhula zimene Yehova wakuuzani.’

Eliya waukitsa mwana ndipo akumupereka kwa mayi ake

“Ganizirani za akhwangwala: Iwo safesa mbewu kapena kukolola. Alibe nkhokwe kapena nyumba yosungiramo zinthu, koma Mulungu amawadyetsa. Kodi inu si amtengo wapatali kuposa mbalame?”​—Luka 12:24

Mafunso: Kodi mayi wamasiye wa ku Zarefati anasonyeza bwanji kuti ankakhulupirira Yehova? Kodi tikudziwa bwanji kuti Eliya analidi mneneri wa Mulungu?

1 Mafumu 17:8-24; Luka 4:25, 26

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena