Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 59 tsamba 142-tsamba 143 ndime 5
  • Anyamata 4 Amene Anamvera Yehova

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anyamata 4 Amene Anamvera Yehova
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Anyamata Anai m’Babulo
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Ayesedwa—Koma Akhulupirikabe kwa Yehova!
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Buku la Danieli ndi Inu
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Yehova Amafupa Chikhulupiriro ndi Kulimba Mtima
    Nsanja ya Olonda—1988
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 59 tsamba 142-tsamba 143 ndime 5
Danieli, Hananiya, Misayeli ndi Azariya akukana kudya chakudya cha mfumu

MUTU 59

Anyamata 4 Amene Anamvera Yehova

Nebukadinezara atatenga akalonga a ku Yuda n’kupita nawo ku Babulo, anasankha nduna ina dzina lake Asipenazi kuti iziyang’anira akalongawo. Nebukadinezara anauza Asipenazi kuti asankhe anyamata athanzi komanso anzeru. Anamuuza kuti anyamatawo asamaliridwe komanso aphunzitsidwe kwa zaka zitatu n’cholinga choti adzakhale akuluakulu a boma ku Babuloko. Anyamata amenewa anayeneranso kuwaphunzitsa kuwerenga, kulemba komanso kulankhula chilankhulo cha Akasidi. Ankafunikanso kumawapatsa chakudya chimene mfumu ndi anthu ogwira ntchito kunyumba kwake ankadya. Pagulu la anyamatawa panali Danieli, Hananiya, Misayeli ndi Azariya. Koma Asipenazi anawapatsa mayina achibabulo akuti, Belitesazara, Shadireki, Misheki ndi Abedinego. Kodi zimene ankawaphunzitsazo zinachititsa kuti anyamatawa asiye kutumikira Yehova? Ayi.

Iwo anatsimikiza kuti apitirizabe kumvera Yehova. Ankadziwa kuti sakuyenera kudya chakudya cha mfumu chifukwa Chilamulo cha Yehova chinkaletsa zina mwa zakudya zimenezo. Choncho anauza Asipenazi kuti: ‘Chonde musamatipatse chakudya cha mfumu.’ Koma Asipenazi anawayankha kuti: ‘Mukapanda kumadya zakudya za mfumu muwonda ndipo mfumu indipha.’

Ndiyeno Danieli anapeza nzeru. Anauza Asipenazi kuti: ‘Muzitipatsa masamba ndi madzi kwa masiku 10. Kenako mudzayerekeze mmene tizidzaonekera ndi mmene anyamata ena azidzaonekera.’ Asipenazi anavomera.

Patatha masiku 10, Danieli ndi anzake atatuwo ankaoneka athanzi kuposa anyamata ena onse. Yehova anasangalala chifukwa choti anyamatawa anamumvera ndipo anapatsa Danieli nzeru moti ankatha kudziwa tanthauzo la masomphenya ndi maloto.

Zaka zitatu zija zitatha Asipenazi anapita ndi anyamata onse kwa Nebukadinezara. Mfumuyo italankhula nawo, anaona kuti Danieli, Hananiya, Sadirake ndi Azariya anali anzeru komanso ochangamuka kuposa anyamata enawo. Choncho anawasankha kuti azigwira ntchito kunyumba kwake. Mfumuyi inkafunsira nzeru kwa anyamatawa chifukwa Yehova anawathandiza kukhala ndi nzeru kuposa anzeru onse a m’dzikolo.

Ngakhale kuti anyamata 4 amenewa ankakhala kudziko la eni, sanaiwale kuti anali anthu a Mulungu. Kodi iwenso utakhala kumalo koti kulibe makolo ako, ungapitirizebe kumvera Yehova?

“Usalole kuti munthu aliyense akuderere poona kuti ndiwe wamngʼono. Mʼmalomwake, ukhale chitsanzo kwa okhulupirika pa zimene umalankhula, makhalidwe ako, chikondi, chikhulupiriro ndi khalidwe loyera.”​—1 Timoteyo 4:12

Mafunso: N’chifukwa chiyani Danieli ndi anzake atatu ankamvera Yehova? Kodi Yehova anawathandiza bwanji?

Danieli 1:1-21

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena