Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 69 tsamba 164-tsamba 165 ndime 2
  • Gabirieli Anaonekera kwa Mariya

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Gabirieli Anaonekera kwa Mariya
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mngelo Afikira Mariya
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Alemekezedwa Asanabadwe
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Yesu Analemekezedwa Asanabadwe
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • “Ndinetu Kapolo wa Yehova!”
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 69 tsamba 164-tsamba 165 ndime 2
Mngelo Gabirieli akuonekera kwa Mariya

MUTU 69

Gabirieli Analankhula ndi Mariya

Mngelo akuonekera kwa Yosefe m’maloto

Elizabeti anali ndi m’bale wake wachitsikana dzina lake Mariya. Iye ankakhala mumzinda wa Nazarete ku Galileya. Mtsikanayu anali pa chibwenzi ndi kalipentala wina dzina lake Yosefe. Ndiyeno patatha miyezi 6 Elizabeti ali woyembekezera, mngelo Gabirieli anapita kwa Mariya n’kumuuza kuti: ‘Moni Mariya. Yehova wakukomera mtima kwambiri.’ Mariya sanamvetse zimene mngeloyu ankatanthauza. Ndiyeno Gabirieli anamuuza kuti: ‘Udzakhala woyembekezera n’kubereka mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina lakuti Yesu. Iye adzakhala Mfumu ndipo Ufumu wake sudzatha.’

Mariya anafunsa kuti: ‘Kodi zimenezi zidzatheka bwanji, chifukwa sindinagonepo ndi mwamuna.’ Gabirieli anamuuza kuti: ‘Mulungu sangalephere kuchita chilichonse. Mzimu woyera udzafika pa iwe ndipo udzakhala ndi mwana. Kodi ukudziwa kuti panopa m’bale wako Elizabeti ndi woyembekezera?’ Zitatero, Mariya anayankha kuti: ‘Ndine kapolo wa Yehova. Zimene mwanenazo zichitike ndithu kwa ine.’

Yosefe akutenga Mariya ali woyembekezera kuti akhale mkazi wake

Mariya anauyamba ulendo wopita kukaona Elizabeti. Pa nthawiyi, Elizabeti ankakhala mumzinda winawake wakumapiri. Atafika, n’kupereka moni, mwana amene anali m’mimba mwa Elizabeti anayamba kudumpha. Ndiyeno Elizabeti anadzazidwa ndi mzimu woyera n’kuyamba kunena kuti: ‘Mariya, Yehova wakudalitsa. Ndi mwayi waukulu kuti mayi wa Ambuye wanga wafika m’nyumba mwanga.’ Mariya anati: ‘Moyo wanga ukulemekeza Yehova.’ Mariya anakhala ndi Elizabeti kwa miyezi itatu ndipo kenako anabwerera kwawo ku Nazareti.

Yosefe atamva zoti Mariya ndi woyembekezera ankafuna kuthetsa chibwenzi. Koma ali m’tulo mngelo anamuuza kuti: ‘Usaope kutenga Mariya kuti akhale mkazi wako chifukwa sanachite choipa chilichonse.’ Choncho Yosefe anatengadi Mariya n’kumakakhala naye kwawo.

“Yehova amachita chilichonse chimene wafuna kumwamba ndi padziko lapansi.”​—Salimo 135:6

Mafunso: Kodi Gabirieli anauza Mariya zinthu ziti zokhudza mwana amene adzabereke? Kodi Elizabeti ndi Mariya anamva bwanji chifukwa cha zimene zinawachitikira?

Mateyu 1:18-25; Luka 1:26-56; Yesaya 7:14; 9:7; Danieli 2:44; Agalatiya 4:4

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena