Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 77 tsamba 182-tsamba 183 ndime 2
  • Yesu Anakumana ndi Mayi Pachitsime

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Anakumana ndi Mayi Pachitsime
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yesu Analalikira Mayi wa ku Samariya
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Kuphunzitsa Mkazi wa ku Samariya
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Ndi Mkazi pa Chitsime
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Madzi Opatsa Moyo
    Galamukani!—2009
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 77 tsamba 182-tsamba 183 ndime 2
Yesu akulankhula ndi mayi wa Chisamariya pachitsime cha Yakobo

MUTU 77

Yesu Anakumana ndi Mayi Pachitsime

Pasika atatha, Yesu ndi ophunzira ake anayamba ulendo wobwerera ku Galileya ndipo anadutsa ku Samariya. Atafika mumzinda wa Sukari, Yesu anaima pachitsime cha Yakobo. Ophunzira ake anamusiya akupuma, n’kupita kukagula chakudya mumzindawo.

Ndiyeno panafika mayi wina kudzatunga madzi. Yesu anamuuza kuti: “Mundigawireko madzi akumwa mayi.” Mayiyo anati: ‘Bwanji mukupempha madzi kwa ine? Inetu ndine Msamariya. Paja Ayuda salankhula ndi Asamariya.’ Koma Yesu anamuuza kuti: ‘Mukanadziwa kuti ndine ndani, bwenzi mutandipempha kuti ndikupatseni madzi amoyo.’ Mayiyo anafunsa Yesu kuti: ‘Mukutanthauza chiyani? Inu mulibe chotungira ndiye madzi muwatenga kuti?’ Yesu anayankha kuti: ‘Aliyense wakumwa madzi amene ine ndingam’patse sadzamvanso ludzu ngakhale pang’ono.’ Ndiyeno mayiyo anati: “Bambo, ndipatseni madzi amenewo.”

Kenako Yesu anauza mayiyo kuti: ‘Pitani mukaitane mwamuna wanu.’ Koma mayiyo anati: “Ndilibe Mwamuna.” Yesu anati: ‘Mwanena zoona. Chifukwa mwakwatiwapo ndi amuna 5, ndipo mwamuna amene mukukhala naye panopa si mwamuna wanu.’ Mayiyo atamva zimenezi anati: ‘Ndazindikira kuti ndinu mneneri. Ife timakhulupirira kuti tiyenera kulambira Mulungu m’phiri ili, pamene Ayudanu mumati tiyenera kulambira Mulungu ku Yerusalemu kokha. Koma ndikukhulupirira kuti Mesiya akadzabwera adzatiphunzitsa kuti tizilambira bwanji.’ Ndiyeno Yesu anamuuza zimene anali asanauzepo aliyense. Anati: ‘Ineyo ndine Mesiya.’

Yesu akulankhula ndi Asamariya

Mayiyo anathamanga n’kukauza Asamariya kuti: ‘Ndakumana ndi Mesiya. Akudziwa zonse zokhudza ineyo. Tiyeni mukamuone.’ Anthuwo anapita naye limodzi ndipo Yesu anawaphunzitsa zinthu zambiri.

Asamariyawo anapempha Yesu kuti akhalebe mumzinda wawo. Choncho anakhala nawo kwa masiku awiri n’kumawaphunzitsa ndipo ambiri anamukhulupirira. Iwo anauza mayi uja kuti: ‘Zimene tamva kwa munthuyo zatithandiza kudziwa kuti iyedi ndi mpulumutsi wa dziko.’

“‘Bwera!’ Komanso aliyense amene akumva ludzu abwere. Aliyense amene akufuna, amwe madzi opatsa moyo kwaulere.”​—Chivumbulutso 22:17

Mafunso: N’chifukwa chiyani mayi wa Chisamariya anadabwa ataona kuti Yesu akulankhula naye? Kodi Yesu anamuuza zinthu ziti?

Yohane 4:1-42

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena