MUTU 88
Yesu Anamangidwa
Yesu ndi atumwi ake anadutsa m’chigwa cha Kidironi n’kupita kuphiri la Maolivi. Apa n’kuti nthawi itapitirira 12 koloko ya usiku ndipo mwezi unali wathunthu. Atafika m’munda wa Getsemane Yesu anauza atumwiwo kuti: “Khalani pansi panopa, ine ndikupita uko kukapemphera.” Kenako anapita chapatali ndipo anagwada n’kuyamba kupemphera. Iye anali ndi nkhawa kwambiri ndipo anapemphera kwa Yehova kuti: “Zimene inu mukufuna zichitike.” Yehova anatumiza mngelo kuti adzalimbikitse Yesu. Atapita pamene panali atumwi paja, anapeza atumwiwo akugona. Iye anawauza kuti: ‘Dzukani! Ino si nthawi yogona. Nthawi yoti ndiperekedwe kwa adani yayandikira.’
Pasanapite nthawi Yudasi anatulukira ali ndi gulu la anthu amene ananyamula malupanga ndi zibonga. Yesu ndi atumwi ake ankakonda kupita kumunda wa Getsemani. Choncho Yudasi ankadziwa kuti Yesu angapezeke kumeneku. Iye anali atauza anthuwo kuti akachita zinazake kuti iwo athe kuzindikira Yesu. Choncho anangofikira pamene panali Yesu n’kunena kuti: ‘Muli bwanji Mphunzitsi?’ Kenako anamukisa. Koma Yesu anati: ‘Yudasi, kodi ukundipereka pondikisa?’
Yesu anayandikira gululo n’kulifunsa kuti: “Mukufuna ndani?” Anthuwo anayankha kuti: “Yesu Mnazareti.” Ndiyeno iye anayankha kuti: “Ndi ineyo.” Koma anthuwo anabwerera m’mbuyo n’kugwa pansi. Yesu anawafunsanso kuti: ‘Ndati mukufuna ndani?’ Iwo anayankhanso kuti: “Yesu Mnazareti.” Yesu anawauza kuti: ‘Ndakuuzani kuti, ndi ineyo. Asiyeni awa azipita.’
Nthawi yomweyo Petulo anasolola lupanga lake n’kudula khutu la Makasi, yemwe anali wantchito wa mkulu wa ansembe. Koma Yesu anatenga khutulo n’kuliika pamalo ake ndipo anamuchiritsa. Kenako anauza Petulo kuti: ‘Bwezera lupangalo pamalo ake. Ukamapha anthu ndi lupanga, nawenso udzaphedwa ndi lupanga.’ Asilikaliwo anagwira Yesu n’kumumanga ndipo atumwi aja anathawa. Kenako asilikaliwo anatenga Yesu n’kupita naye kwa wansembe wamkulu, dzina lake Anasi. Atamufunsa mafunso anamutumiza kwa mkulu wa ansembe, dzina lake Kayafa. Koma kodi atumwi aja zinawathera bwanji?
“Mʼdzikomu mukumana ndi mavuto aakulu, koma limbani mtima. Ine ndaligonjetsa dziko.”—Yohane 16:33