Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lff phunziro 8
  • Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu
  • Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • FUFUZANI MOZAMA
  • ZOMWE TAPHUNZIRA
  • ONANI ZINANSO
  • Kodi Tingapeze Bwanji Anzathu Abwino?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake
    Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Muzisankha Mwanzeru Anthu Ocheza Nawo
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Ndingadziwe Bwanji Anzanga Enieni?
    Galamukani!—2011
Onani Zambiri
Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
lff phunziro 8
Phunziro 8. Munthu wakhala pabenchi ndipo akuyang’ana kumwamba.

PHUNZIRO 08

Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu

Losindikizidwa
Losindikizidwa
Losindikizidwa

Yehova akufuna kuti mumudziwe bwino. Chifukwa chiyani? Amaona kuti mukadziwa bwino makhalidwe ake, mmene amachitira zinthu komanso cholinga chake mungafunitsitse kukhala mnzake. Koma kodi mukuona kuti n’zothekadi kuti inuyo mukhale mnzake wa Mulungu? (Werengani Salimo 25:14.) Kodi mungatani kuti mukhale mnzake wa Mulungu? Baibulo limayankha mafunso amenewa ndipo limasonyeza kuti kukhala mnzake wa Yehova n’kofunika kwambiri kuposa kugwirizana ndi munthu wina aliyense.

1. Kodi Yehova akukupemphani kuti muchite chiyani?

Baibulo limanena kuti “Yandikirani Mulungu ndipo iyenso adzakuyandikirani.” (Yakobo 4:8) Kodi mawu amenewa akutanthauza chiyani? Yehova akukupemphani kuti mukhale mnzake. Anthu ena amaona kuti n’zosatheka kuti Mulungu akhale mnzawo chifukwa sangathe kumuona. Koma m’Baibulo, Yehova amafotokoza zonse zotithandiza kuti tidziwe makhalidwe ake n’cholinga choti tikhale anzake. Tikamawerenga uthenga umene Yehova watipatsa m’Baibulo, ubwenzi wathu ndi iye umalimba kwambiri ngakhale kuti sitinamuonepo.

2. N’chifukwa chiyani tinganene kuti Yehova akhoza kukhala Mnzanu wabwino kwambiri kuposa wina aliyense?

Tikutero chifukwa chakuti Yehova amakukondani kwambiri kuposa munthu wina aliyense. Iye amafuna kuti muzisangalala ndiponso kuti muzipemphera kwa iye nthawi zonse mukakumana ndi mavuto. Baibulo limati muzimutulira “nkhawa zanu zonse, chifukwa amakufunirani zabwino.” (1 Petulo 5:7) Yehova ndi wokonzeka kuthandiza, kutonthoza ndiponso kumvetsera anzake akamalankhula.​—Werengani Salimo 94:18, 19.

3. Kodi Yehova amafuna kuti anzake azichita chiyani?

N’zoona kuti Yehova amakonda anthu onse, “koma anthu owongoka mtima [ndi amene] amakhala nawo pa ubwenzi wolimba.” (Miyambo 3:32) Yehova amafuna kuti anzake aziyesetsa kuchita zinthu zimene iye amaziona kuti ndi zabwino, n’kumapewa zinthu zimene iye amaziona kuti n’zoipa. Anthu ena amaona kuti sangakwanitse kuchita zinthu zonse zimene Yehova amafuna komanso kupeweratu zoipa zonse. Koma Yehova ndi Mulungu wachifundo. Iye amalola kuti munthu aliyense amene amamukonda ndi mtima wonse komanso amene amayesetsa kuchita zinthu zomusangalatsa akhale mnzake.​—Salimo 147:11; Machitidwe 10:34, 35.

FUFUZANI MOZAMA

Onani zina zimene mungachite kuti Yehova akhale mnzanu ndiponso chifukwa chake iye angakhale Mnzanu wabwino kwambiri kuposa wina aliyense.

4. Abulahamu anali mnzake wa Yehova

Nkhani ya m’Baibulo yokhudza Abulahamu (yemwe ankadziwikanso kuti Abulamu) imatithandiza kudziwa zimene zimafunika kuti munthu akhale mnzake wa Mulungu. Werengani nkhani ya Abulahamu pa Genesis 12:1-4. Kenako mukambirane mafunso otsatirawa:

  • Kodi Yehova anauza Abulahamu kuti achite chiyani Abulahamu?

  • Kodi Yehova anamulonjeza chiyani?

  • Kodi Abulahamu anachita chiyani atamva malangizo a Yehova?

5. Zimene Yehova amafuna kuti anzake azichita

Nthawi zambiri timafuna kuti anzathu azichita zinthu zinazake.

  • Kodi inuyo mumafuna kuti anzanu azikuchitirani zinthu ziti?

Werengani 1 Yohane 5:3, kenako mukambirane funso ili:

  • Kodi Yehova amafuna kuti anzake azichita chiyani?

Kuti timvere Yehova, tingafunike kusintha zinthu zina zimene timachita kapena khalidwe lathu. Werengani Yesaya 48:17, 18, kenako mukambirane funso ili:

  • N’chifukwa chiyani Yehova amafuna kuti anzake asinthe zinthu zina?

Wogwira ntchito yomanga akupatsira mnzake chipewa choteteza kumutu.

Mnzathu wabwino amatiuza zinthu zimene zingatiteteze komanso kutithandiza. Yehova amachitanso chimodzimodzi kwa anzake

6. Zimene Yehova amachita kuti athandize anzake

Yehova amathandiza anzake kupirira mavuto. Onerani VIDIYO, kenako mukambirane funso ili:

VIDIYO: Yehova Wandichitira Zambiri (3:20)

  • Muvidiyoyi, kodi Yehova anathandiza bwanji mayi wina kulimbana ndi maganizo oipa?

Werengani Yesaya 41:10, 13, kenako mukambirane mafunso otsatirawa:

  • Kodi Yehova akulonjeza kuti adzawachitira chiyani anzake onse?

  • Kodi mukuganiza kuti Yehova akhoza kukhala Mnzanu wabwino? N’chifukwa chiyani mukutero?

Zithunzi: Mabwenzi akuthandizana. 1. Mzibambo akuthandiza mnzake kusuntha tebulo lalikulu. 2. Mzimayi akuuza mnzake zakukhosi. 3. Mzibambo akuthandiza mnzake yemwe akuyendera ndodo.

Anzanu apamtima amakuthandizani mukafunika thandizo. Nayenso Yehova adzakuthandizani

7. Kuti Yehova akhale mnzathu, tiyenera kulankhulana

Kulankhulana kumalimbitsa ubwenzi wathu ndi Yehova. Werengani Salimo 86:6, 11, kenako mukambirane mafunso awa:

  • Kodi tingalankhule bwanji ndi Yehova?

  • Kodi Yehova amalankhula nafe bwanji?

Zithunzi: 1. Mzimayi akupemphera. Pamwamba pa mutu wake pali muvi woloza kumwamba. 2. Mzimayi akuwerenga Baibulo. Pamwamba pa mutu wake pali muvi woloza pansi.

Timalankhula ndi Yehova m’pemphero; iye amalankhula nafe kudzera m’Baibulo

ANTHU ENA AMANENA KUTI: “N’zosatheka kukhala mnzake wa Mulungu.”

  • Kodi mungagwiritse ntchito lemba liti posonyeza kuti n’zotheka kukhala mnzake wa Yehova?

ZOMWE TAPHUNZIRA

Yehova akufuna kuti mukhale Mnzake, ndipo iye akuthandizani kuchita zimenezi.

Kubwereza

  • Kodi Yehova amathandiza bwanji anzake?

  • N’chifukwa chiyani Yehova amauza anzake kuti asinthe zinthu zina?

  • Kodi mukuganiza kuti Yehova amafuna kuti anzake azichita zinthu zomwe sangakwanitse? N’chifukwa chiyani mukutero?

Zoti Muchite

ONANI ZINANSO

Kodi kukhala mnzake wa Mulungu kungakuthandizeni bwanji?

“Yehova Ndiye Mulungu Wofunika Kum’dziwa” (Nsanja ya Olonda, February 15, 2003)

Onani zimene mungachite kuti Mulungu akhale mnzanu.

“Kodi Ndingatani Kuti Ndikhale Paubwenzi ndi Mulungu?” (Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri, mutu 35)

Onani chifukwa chake mayi wina amaona kuti kukhala mnzake wa Yehova kunapulumutsa moyo wake.

“Sindinkafuna Kufa!” (Nsanja ya Olonda Na. 1 2017)

Mvetserani pamene achinyamata akufotokoza mmene amaonera Yehova.

Kodi Kukhala Bwenzi la Mulungu Kumatanthauza Chiyani? 1:​46

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena