Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w95 1/15 tsamba 8-9
  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Puerto Rico

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Puerto Rico
  • Nsanja ya Olonda—1995
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Munda Watsopano
  • Muziona Kuti Abale ndi Alongo Anu Osamva Ndi Ofunika Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Puerto Rico Dziko Lachuma M’dera Lotentha
    Galamukani!—2008
  • Kumvetsera ndi Maso Anu
    Galamukani!—1998
  • Ndakhala Moyo Wosangalala Chifukwa Chothandiza Ena
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1995
w95 1/15 tsamba 8-9

Mboni za Yehova Padziko Lonse​—Puerto Rico

PAKATI pa Caribbean Sea ndi Atlantic Ocean pali chisumbu chobiriŵira, chotentha cha Puerto Rico. Christopher Columbus ananena kuti chinali cha Spain mu 1493 ndipo anachitcha San Juan Bautista pokumbukira Yohane Mbatizi. Mzinda wake waukulu unatchedwa Puerto Rico kwanthaŵi yaitali, kapena “Doko Lolemera.” M’kupita kwa nthaŵi, dzinali linagwiritsiridwa ntchito kutchula chisumbu chonsecho, pamene kuli kwakuti mzindawo unadzatchedwa San Juan.

Puerto Rico wakhaladi doko lolemera m’njira zambiri. Golidi wambiri anatumizidwa panyanja kumka kwina kuchokera kunoko m’zaka zoyambirira za ulamuliro wa Aspanya. Tsopano chisumbucho chimatumiza kunja nzimbe, khofi, nthochi, ndi zipatso, ngakhale kuti maindasitale ake opanga zinthu ndi a ntchito zina ndiwo amene amadzetsa chuma chake chambiri lerolino. Komabe, Puerto Rico wakhaladi doko lolemera m’lingaliro linanso lofunika koposa.

Mbiri yabwino yonena za Ufumu wa Mulungu inayamba kulalikidwa kunoko m’ma 1930. Lerolino, mu Puerto Rico muli ofalitsa mbiri yabwino oposa 25,000. Mu 1993 antchito a panthambiyi ya Watch Tower Society anawonjezereka kuchokera pa 23 kufikira pa oposa 100. Chiwonjezeko chimenechi chinali chofunika kotero kuti nthambiyo iyang’anire kutembenuzidwa kwa mabuku ofotokoza Baibulo m’Chispanya, ikumachititsa zofalitsidwazo kukhala zopezeka kwa anthu pafupifupi 350,000,000 olankhula Chispanya padziko lonse.

Munda Watsopano

Ofesi yanthambi ikusimbanso kuti: “Munda watsopano watseguka mu Puerto Rico chifukwa chakuti takhala tikupanga zoyesayesa kutengera uthenga wa Ufumu kwa anthu ogontha. Mlongo wina akusimba za chokumana nacho chotsatirachi: ‘Ndinali kugwira ntchito pakati pa anthu ogontha ndipo ndinafikira mkazi wina wokhala ndi ana aŵiri aang’ono. Pamene anazindikira kuti ndinali Mboni, anakana kulankhula nane nthaŵi yomweyo chifukwa chakuti mwamuna wake, amenenso anali wogontha, sanakonde Mboni za Yehova.

“‘Miyezi ingapo pambuyo pake mkazi mmodzimodziyu anachezera bwenzi lake lina limene linali kuphunzira Baibulo ndi Mboni. Iye anagwirizana nawo m’phunzirolo ndipo anasangalala nalo kwambiri. Ndinapita kwa mkaziyo kachiŵirinso, ndipo iye anabwereza kunena kuti mwamuna wake samakonda Mboni. Komabe, iye anafuna kumvetsetsa Baibulo ndipo anali atatopa ndi tchalitchi chake chifukwa chakuti sankaphunzira chilichonse. Tinayamba kuphunzira, tikumagwiritsira ntchito trakiti. Tsiku lina iye anandiuza kuti ndibwerenso pa Loŵeruka chifukwa chakuti mwamuna wake adzakhalapo. “Komatu paja samatikonda, kodi sichoncho?” ndinafunsa motero. Iye anayankha kuti: “Akufuna kudziŵa za nkhani yake yonse.”

“‘Aŵiri onsewo anali kugogoda pa khomo panga tsiku lotsatira! Popeza kuti mwamunayo anali ndi mafunso ambiri, ndinawaitanira ku misonkhano yathu ya anthu ogontha. Iye anafika kumeneko ine ndisanafike ndipo kuyambira pamenepo sanaphonyepo msonkhano. Akulalikira kwa anthu ena ogontha, wafika pamsonkhano wadera, ndipo akuyembekezera ubatizo.’”

Lipoti la nthambiyo likupitirizabe kuti: “Pamsonkhano wathu wachigawo chaka chino, programu yonseyo inaperekedwa m’chinenero chamanja, anthu ambirimbiri ogontha analipo ndi mabanja awo. Nthaŵi yotenga mtima inafika mkati mwa nkhani yotsiriza pamene wolankhula wake anatchula za ntchito imene ikuchitidwa pakati pa anthu ogontha ndi kuti pafupifupi 70 analipo. Panali chikondwerero chachikulu, koma, monga momwe wolankhulayo anaonera, anthu ogonthawo sanachione. Chotero akumapempha anthu ogonthawo kuyang’ana omvetsera onse, wolankhulayo anabwerezanso funso lake kuti, ‘Kodi muli achimwemwe kukhala ndi abale anu ogontha pano?’ ndipo anapempha omvetserawo kusonyeza chikondwerero mwa kugwedeza m’mwamba mikono yonse. Kunali kokondweretsa kwambiri kuona abale ndi alongo 11,000 akumakondwera mwa kugwedeza manja awo. Abale ndi alongo athu ogonthawo anali okondwa kwambiri ndipo anadziona kukhala ali mbali ya ubale waukulu. Ambiri anakhetsa misozi yachisangalalo.”

Pamene Mboni za Yehova zikukhala ndi phande m’ntchito ya kututa ku Puerto Rico, mosakayikira dzikolo lidzapitirizabe kukhala doko lolemera. “Nkhosa” za Mulungu zimene iye amatcha kuti “zofunika za amitundu onse,” zidzapitirizabe kufika kotero kuti nyumba ya Yehova idzazidwe ndi ulemerero.​—Yohane 10:16; Hagai 2:7.

[Bokosi patsamba 9]

ZIŴERENGERO ZA DZIKOLO

Chaka Chautumiki cha 1994

CHIŴERENGERO CHAPAMWAMBA CHA OCHITIRA UMBONI: 25,428

KUGAŴA: Mboni 1 pa anthu 139

OFIKA PA CHIKUMBUTSO: 60,252

AVAREJI YA OFALITSA AUPAINIYA: 2,329

AVAREJI YA MAPHUNZIRO A BAIBULO: 19,012

CHIŴERENGERO CHA OBATIZIDWA: 919

CHIŴERENGERO CHA MIPINGO: 312

OFESI YA NTHAMBI: GUAYNABO

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena