Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w04 3/15 tsamba 3
  • Mwambo wa Chikumbutso Umene Ukukukhudzani

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mwambo wa Chikumbutso Umene Ukukukhudzani
  • Nsanja ya Olonda—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Chakudya Chamadzulo cha Ambuye Ndi Mwambo Umene Umalemekeza Mulungu
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • “Muzichita Zimenezi Pondikumbukira”
    Nsanja ya Olonda—2013
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kuchita Chikumbutso cha Mgonero wa Ambuye?
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Kodi Mgonero wa Ambuye Tiziukumbukira Motani?
    Nsanja ya Olonda—2004
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2004
w04 3/15 tsamba 3

Mwambo wa Chikumbutso Umene Ukukukhudzani

YESU KRISTU ali padziko lapansi anakhazikitsa mwambo wa chikumbutso umene umalemekeza Mulungu. Umenewu ndi mwambo wa chipembedzo umodzi wokha umene iye analamulira ophunzira ake mwachindunji kuti azikumbukira. Ndi mwambo wa Mgonero wa Ambuye, umene umatchedwanso Mgonero Womaliza.

Tayerekezani kuti mwafika pa mwambowo popanda aliyense kudziŵa ndipo mukuonerera zimene zikuchitika mpaka pamene mwambowu ukuyambika. Yesu ndi atumwi ake asonkhana pamodzi m’chipinda chapamwamba ku Yerusalemu kuti akondwerere Paskha Wachiyuda. Amaliza kudya chakudya chimene anthu amadya nthaŵi zonse pa Paskha, chomwe ndi nyama ya nkhosa yowotcha, masamba owawa, mkate wopanda chotupitsa, ndi vinyo wofiira. Yudasi Iskariote, mtumwi wosakhulupirika, watulutsidwa ndipo pasanapite nthaŵi yaitali adzapereka Mbuye wakeyo kwa adani. (Mateyu 26:17-25; Yohane 13:21, 26-30) M’chipindamo mwatsala Yesu ndi atumwi ake okhulupirika 11. M’modzi mwa iwo ndi Mateyu.

Malinga ndi nkhani ya Mateyu imene analemba monga mboni yoona ndi maso, Yesu anakhazikitsa Mgonero wa Ambuye motere: “Yesu anatenga mkate [wopanda chotupitsa], nadalitsa, naunyema; ndipo mmene anapatsa kwa ophunzira, anati, Tengani, idyani; ichi ndi thupi langa. Ndipo pamene anatenga chikho [mmene munali vinyo], anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ichi inu nonse, pakuti ichi ndicho mwazi wanga wa pangano, wothiridwa chifukwa cha anthu ambiri ku kuchotsa machimo.”​—Mateyu 26:26-28.

N’chifukwa chiyani Yesu anakhazikitsa Mgonero wa Ambuye? N’chifukwa chiyani pochita zimenezo anagwiritsa ntchito mkate wopanda chotupitsa ndi vinyo wofiira? Kodi otsatira onse a Kristu anafunika kudya nawo zizindikirozi? Kodi mgonerowu unafunika kuti ophunzirawo aziukumbukira kangati? Ndipo kodi ulidi ndi tanthauzo kwa inu?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena