Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w05 7/1 tsamba 27
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
  • Nsanja ya Olonda—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Buku la Levitiko Limatiphunzitsa Mmene Tingachitire Zinthu ndi Ena
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda—2006
  • ‘Malamulo a Yehova Ndi Angwiro’
    Yandikirani Yehova
  • “Mukhale Oyera”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2005
w05 7/1 tsamba 27

Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Lemba la Deuteronomo 14:21 limati: “Musamadya chinthu chilichonse chitafa chokha.” Kodi zimenezi zikutsutsana ndi lemba la Levitiko 11:40, lomwe limanena kuti: “Iye wakudya kanthu ka mtembo wake azitsuka zovala zake, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo”?

Mavesi awiri amenewa sakutsutsana. Lemba loyambalo likungobwereza lamulo loletsa kudya nyama yomwe yapezeka itafa, mwinamwake imene yaphedwa ndi zilombo zakuthengo. (Eksodo 22:31; Levitiko 22:8) Lemba lachiwirili likufotokoza zimene Mwisrayeli akanachita ngati mwinamwake mwangozi waswa lamulo limeneli.

Ngakhale kuti Chilamulo chinali kuletsa kuchita zinthu zina, nthawi zina anthu anali kunyalanyaza malamulowo. Mwachitsanzo, panali malamulo oletsa kuba, kupha, kupereka umboni wonama, ndi ena otero. Panthawi imodzimodziyo, anatchulanso zilango zimene woswa malamulo operekedwa ndi Mulungu amenewa anafunika kulandira. Zilango zimenezo zinapatsa mphamvu malamulowo ndi kusonyeza kuwopsa kwake.

Munthu akaswa lamulo loletsa kudya nyama yofa yokha anali wodetsedwa pamaso pa Yehova ndipo anafunikira kutsatira njira yoyenera ya kudziyeretsa. Koma akalephera kudziyeretsa moyenerera, anali ‘kusenza mphulupulu yake.’​—Levitiko 17:15, 16.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena