Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w05 9/15 tsamba 29
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
  • Nsanja ya Olonda—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ndiyenera Kuchita Maseŵero Apakompyuta Kapena Apavidiyo?
    Galamukani!—1996
  • Kodi Ndizichita Masewera a Pakompyuta?
    Galamukani!—2008
  • Kodi Ndiyenera Kuchita Masewera a Pakompyuta?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
  • Kodi Ndiyenera Kudziwa Zotani Zokhudza Kusewera Magemu a Pazipangizo Zamakono?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2005
w05 9/15 tsamba 29

Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Kodi kusewera masewera achiwawa a pakompyuta kungam’sokonezere munthu ubwenzi wake ndi Yehova?

Mfumu Davide ya Israyeli wakale inati: “Yehova ayesa wolungama mtima: koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.” (Salmo 11:5) Mawu a Chihebri otanthauza ‘kuda’ amatanthauzanso “kukhala mdani.” Motero munthu aliyense amene amakonda zachiwawa akudzipangitsa yekha kukhala mdani wa Mulungu. Choncho funso limene tiyenera kuliganizira ndi ili: Kodi kuchita masewera enaake pakompyuta kungayambitse munthu kukonda zachiwawa?

Masewera achiwawa a pakompyuta amalimbikitsa wosewerayo kugwiritsira ntchito zida zankhondo. Nthawi zambiri masewerawa amaphunzitsa munthuyo nkhondo. Magazini yotchedwa The Economist inanena kuti: “Gulu la asilikali a dziko la United States layamba kudalira kwambiri masewera a pakompyuta pophunzitsa asilikali ake nkhondo. Masewera ena amene asilikaliwa amagwiritsira ntchito amawagula m’masitolo a anthu wamba.”

N’zoona kuti anthu amene amachita masewera achiwawa a pakompyuta sikuti amakhala akuvulazadi anthu enieni. Komabe, kodi kukonda masewera oterewa kumasonyeza kuti mtima wawo ndi wotani? (Mateyu 5:21, 22; Luka 6:45) Kodi munthu wokonda kubaya, kuwombera, kupundula, ndiponso kupha anthu osakhala enieni, mungati ndi wotani? Nanga mungam’ganizire chiyani munthuyu ngati nthawi zambiri mlungu uliwonse amakhala akusangalala pochita masewera achiwawa oterewa, mpaka kufika pomulowerera kwambiri? Ndithu sikulakwa kuganiza kuti munthuyu wayamba kukonda zachiwawa, monga mmene mungadziwire kuti munthu wayamba kukonda zadama ngati akukonda kuona zithunzi zolaula.​—Mateyu 5:27-29.

Kodi Yehova amamuona motani munthu wokonda zachiwawa? Mawu a Davide aja amasonyeza kuti Yehova amadana kwambiri ndi anthu otero. M’masiku a Nowa, Yehova anasonyeza kuti amadana kwambiri ndi anthu okonda zachiwawa. Iye anauza Nowa kuti: “Chimaliziro chake cha anthu onse chafika pamaso panga; pakuti dziko lapansi ladzala ndi chiwawa chifukwa cha iwo; taonani, ndidzawononga iwo pamodzi ndi dziko lapansi.” (Genesis 6:13) Mulungu woona anawononga dziko lonse la anthu la panthawiyo chifukwa cha zochita zawo zachiwawa. Iye anasiyako Nowa yekha ndi am’banja mwake, ndipo onse pamodzi analipo anthu eyiti okha amene sankakonda zachiwawa.​—2 Petro 2:5.

Anthu ofuna kukhala mabwenzi a Yehova ‘amasula malupanga awo akhale zolimira.’ M’malo mophunzira kukonda zachiwawa, iwo ‘saphunziranso nkhondo.’ (Yesaya 2:4) Kuti tizigwirizanabe ndi Mulungu, osadana naye, tiyenera ‘kupatuka pazoipa, n’kumachita zabwino.’ Tiyenera ‘kufunafuna mtendere ndi kuulondola.’​—1 Petro 3:11.

Nanga tingatani ngati tinazolowera kale masewerawa? Poti Yehova amadana nawo, tiyesetse kupewa masewerawa kuti tim’sangalatse. Ndithu, tiyenera kupemphera kuti mzimu woyera wa Mulungu utithandize kusiya khalidwe limeneli, lomwe limasokoneza munthu mwauzimu. Tingathe kulisiya pokhala anthu abwino, amtendere, ndiponso odziletsa, n’cholinga chakuti moyo wathu ukhale wogwirizana ndi malamulo a Mulungu.​—Luka 11:13; Agalatiya 5:22, 23.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena