Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w06 1/15 tsamba 3
  • Kodi Angelo Ndani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Angelo Ndani?
  • Nsanja ya Olonda—2006
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Angelo Ndi Otani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Angelo—Kodi Amayambukira Moyo Wanu?
    Nsanja ya Olonda—1987
  • Angelo Ndiwo “Mizimu Yotumikira Anthu”
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Mmene Angelo Amatikhudzira
    Nsanja ya Olonda—2006
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2006
w06 1/15 tsamba 3

Kodi Angelo Ndani?

MFUMU ya ufumu wamphamvu kwambiri sinakhulupirire zimene inali kuona. Amuna atatu omwe anawalamula kuti aphedwe m’ng’anjo ya moto anali atapulumutsidwa ku imfa yochititsa manthayo. Kodi ndani anawapulumutsa? Mfumuyi inauza anthu opulumukawo kuti: “Alemekezedwe [Mulungu wanu], amene anatuma mthenga wake, napulumutsa atumiki ake om’khulupirira iye.” (Danieli 3:28) Mfumu ya Babuloyi, imene inakhalapo zaka zoposa 2000 zapitazo, inadzionera yokha mngelo atapulumutsa anthu. Anthu ambiri kalelo ankakhulupirira angelo. Masiku ano anthu ambiri amakhulupirira kuti angelo alipo, komanso amadziwa kuti angelowo amakhudza moyo wawo m’njira inayake. Kodi angelo ndani, ndipo kodi anakhalako bwanji?

Baibulo limanena kuti, angelo ndi mizimu monga Mulungu. (Salmo 104:4; Yohane 4:24) Angelo alipo ambiri kwabasi moti amatha kukwana mamiliyoni ambirimbiri. (Chivumbulutso 5:11) Ndiponso angelo onse ali ndi “mphamvu zolimba.” (Salmo 103:20) Ngakhale kuti angelo ali ndi umunthu ndiponso anapatsidwa mwayi wosankha zinthu, iwo sanawalenge ngati anthu. Ndipotu, Mulungu analenga angelo kalekale anthu asanakhaleko, ngakhale dziko lapansili asanalilenge. Baibulo limati, pamene Mulungu ‘anaika maziko a dziko lapansi, nyenyezi za m’mawa [kapena kuti angelo] zinaimba limodzi mokondwera, ndi ana onse a Mulungu anafuula ndi chimwemwe.’ (Yobu 38:4, 7) Popeza kuti Mulungu ndiye analenga angelo, iwo amatchedwa ana a Mulungu.

Kodi Mulungu analenga angelo n’cholinga chotani? Kodi ndi ntchito yotani, ngati ilipo n’komwe, imene angelo akhala akugwira pamoyo wa anthu? Kodi angelo amakhudza moyo wathu panopa? Popeza kuti angelo anawalenga ndi ufulu wosankha zochita, kodi pali angelo ena amene anatsatira Satana Mdyerekezi n’kudzipanga kukhala adani a Mulungu? Baibulo lili ndi mayankho oona a mafunso amenewa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena