Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w09 4/1 tsamba 7-8
  • Kodi Kubadwa Mwatsopano Kuli N’cholinga Chotani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Kubadwa Mwatsopano Kuli N’cholinga Chotani?
  • Nsanja ya Olonda—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ndani Amene Amapita Kumwanba, ndipo Nchifukwa Ninji?
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Ulamuliro wa Anthu Ochepa Udzabweretsa Madalitso kwa Anthu Ambiri
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2009
w09 4/1 tsamba 7-8

Kodi Kubadwa Mwatsopano Kuli N’cholinga Chotani?

ANTHU ambiri amaganiza kuti munthu ayenera kubadwanso kuti adzalandire chipulumutso. Koma taonani zimene Yesu ananena zokhudza cholinga cha kubadwa mwatsopano. Iye anati: “Munthu sangathe kuona ufumu wa Mulungu atapanda kubadwanso.” (Yohane 3:3) Choncho, munthu ayenera kubadwanso kuti akalowe mu Ufumu wa Mulungu osati kuti adzapeze chipulumutso. Komabe, ena anganene kuti mawu akuti kulowa mu Ufumu ndiponso kupeza chipulumutso akutanthauza chinthu chimodzi. Koma zimenezi si zoona. Kuti timvetse kusiyana kwake, tiyeni tikambirane kaye tanthauzo la mawu akuti “Ufumu wa Mulungu.”

Ufumu ndi boma, ndipo mawu akuti “Ufumu wa Mulungu” akutanthauza “boma la Mulungu.” Baibulo limatiuza kuti Yesu Khristu, yemwe amatchedwanso “mwana wa munthu,” ndi Mfumu ya Ufumu wa Mulungu ndipo palinso ena amene adzalamulire naye. (Danieli 7:1, 13, 14; Mateyo 26:63, 64) Kuwonjezera pamenepa, masomphenya amene mtumwi Yohane anaona amasonyeza kuti anthu amene adzalamulire ndi Khristu amasankhidwa kuchokera “mu fuko lililonse, lilime, mtundu, ndi dziko lililonse,” ndipo “adzalamulira dziko lapansi monga mafumu.” (Chivumbulutso 5:9, 10; 20:6) Mawu a Mulungu amatiuzanso kuti anthu amene adzalamulire monga mafumu amapanga “kagulu” ka anthu okwana 144,000 “amene anagulidwa padziko lapansi.”​—Luka 12:32; Chivumbulutso 14:1, 3.

Kodi likulu la Ufumu wa Mulungu lili kuti? “Ufumu wa Mulungu” umatchedwanso “ufumu wa kumwamba.” Zimenezi zikusonyeza kuti Yesu limodzi ndi olamulira anzake amalamulira kuchokera kumwamba. (Luka 8:10; Mateyo 13:11) Choncho, Ufumu wa Mulungu ndi boma la kumwamba lolamulidwa ndi Yesu Khristu pamodzi ndi olamulira anzake osankhidwa kuchokera mwa anthu.

Nanga kodi Yesu ankatanthauza chiyani pamene anati munthu ayenera kubadwanso kuti “akalowe mu Ufumu wa Mulungu”? Ankatanthauza kuti munthu ayenera kubadwanso kuti akalamulire ndi Khristu kumwamba. Choncho, cholinga cha kubadwa mwatsopano ndicho kukonzekeretsa kagulu ka anthu amenewa kuti ayenerere kukalamulira kumwamba.

Pofika pano, taona kuti kubadwa mwatsopano n’kofunika kwambiri, kumachititsidwa ndi Mulungu, ndiponso kuti kumakonzekeretsa kagulu ka anthu kuti ayenerere kukalamulira kumwamba. Koma kodi chimachitika n’chiyani kuti munthu abadwe mwatsopano?

[Mawu Otsindika patsamba 7]

Cholinga cha kubadwa mwatsopano ndicho kukonzekeretsa kagulu ka anthu kuti ayenerere kukalamulira kumwamba

[Chithunzi patsamba 7]

Yesu Khristu pamodzi ndi olamulira anzake osankhidwa kuchokera mwa anthu ndi amene amapanga Ufumu wa Mulungu

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena