Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 8/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Pemphero Lingakuthandizeni Kukhala pa Ubwenzi ndi Mulungu
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Tili Ndi Mwayi Wopemphera kwa Mulungu
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Mapemphero Amene Amayankhidwa
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Kodi Ndimapemphero Ayani Omwe Amayankhidwa?
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 8/1 tsamba 16
[Chithunzi patsamba 16]

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Mulungu amamva mapemphero onse?

Mulungu amamva aliyense akamapemphera. (Salimo 145:18, 19) Mawu ake, omwe ndi Baibulo, amatilimbikitsa kuti tizimuuza chilichonse chomwe chimatidetsa nkhawa. (Afilipi 4:6, 7) Koma pali mapemphero ena amene Mulungu samasangalala nawo. Mwachitsanzo, samafuna kuti anthu azinena mapemphero ochita kuloweza.—Werengani Mateyu 6:7.

Yehova samvetseranso mapemphero a anthu amene samvera malamulo ake mwadala. (Miyambo 28:9) Mwachitsanzo, kale kwambiri, Mulungu anakana kumvetsera mapemphero a Aisiraeli amene anali ndi mlandu wakupha anthu. Zimenezi zikusonyeza kuti pali zinthu zimene tiyenera kuchita kuti Mulungu azimva mapemphero athu.—Werengani Yesaya 1:15.

Kodi tizitani kuti Mulungu azimva mapemphero athu?

Mulungu sangamve mapemphero athu ngati tilibe chikhulupiriro. (Yakobo 1:5, 6) Koma tiyenera kukhulupirira kuti Mulungu aliko komanso kuti amatidera nkhawa. Tikhoza kulimbitsa chikhulupiriro chathu tikamaphunzira Baibulo chifukwa munthu amakhala ndi chikhulupiriro cholimba ngati ali ndi umboni wodalirika womwe umapezeka Baibulo.—Werengani Aheberi 11:1, 6.

Tiyeneranso kupemphera kuchokera pansi pa mtima komanso modzichepetsa chifukwa ngakhale Yesu ankapemphera modzichepetsa. (Luka 22:41, 42) Choncho, m’malo momangomuuza Mulungu zoti atichitire, tiziyesetsa kuwerenga Baibulo kuti tizidziwa zimene amafuna. Zimenezi zingatithandize kuti tizipemphera mogwirizana ndi chifuniro chake.—Werengani 1 Yohane 5:14.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 17 wa buku ili, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mukhozanso kupanga dawunilodi pa www.jw.org

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena