Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w14 10/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2014
w14 10/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

N’chifukwa chiyani tiyenera kupemphera kuti Ufumu wa Mulungu ubwere?

Yesu ali pa hatchi kukagonjetsa adani a Ufumu wa Mulungu

Kodi mukufuna kudziwa zambiri zokhudza Ufumu wa Mulungu komanso zimene udzachite?

Ufumu wa Mulungu ndi boma lakumwamba. Yesu anauza otsatira ake kuti azipemphera kuti Ufumuwu ubwere, chifukwa ukadzabwera udzachititsa kuti padzikoli pakhale chilungamo komanso mtendere. Palibe boma la anthu limene lingathetseretu chiwawa, kupanda chilungamo kapena matenda. Ufumu wa Mulungu wokha ndi umene udzathetseratu mavuto amenewa. Mulungu anasankha mwana wake, Yesu, kuti akhale Mfumu ya Ufumu umenewu. Mulungu wasankhanso otsatira ena a Yesu kuti adzalamulire naye limodzi.—Werengani Luka 11:2; 22:28-30.

Posachedwapa, Ufumu wa Mulungu udzawononga onse amene amatsutsa ulamuliro wa Mulungu. Choncho tikamapemphera kuti Ufumu wa Mulungu ubwere, timakhala tikupempha kuti Ufumuwu udzalowe m’malo mwa maufumu omwe alipowa.—Werengani Danieli 7:13, 14; Chivumbulutso 11:15, 18.

N’chifukwa chiyani tingati Ufumu wa Mulungu ndi wabwino kwambiri?

Yesu ndi Mfumu yabwino kwambiri chifukwa ndi wachifundo. Popeza ndi Mwana wa Mulungu, iye ali ndi mphamvu zothandiza anthu onse amene amapempha Mulungu kuti awathandize.—Werengani Salimo 72:8, 12-14.

Ufumu wa Mulungu udzathandiza anthu onse amene amafunadi kuti Ufumuwu ubwere komanso amene amayesetsa kuchita zimene Mulungu amafuna. Mungapindule kwambiri ngati mutaphunzira zimene Baibulo limanena zokhudza Ufumu wa Mulungu.—Werengani Luka 18:16, 17; Yohane 4:23.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 8 m’buku lakuti Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Bukuli likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena