Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 1/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Nyama
    Galamukani!—2015
  • Kodi Zinyama Zimapita Kumwamba?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Mulungu Amasamalira Nyama?
    Galamukani!—2011
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 1/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

N’chifukwa chiyani anthu ambiri amakhulupirira kuti pali winawake amene analenga zonse?

Mayi akuyang’ana mwana wake mosangalala

Moyo ndi wodabwitsa

Zaka 3,000 zapitazo, wolemba ndakatulo wina anati: “Munandipanga modabwitsa ndipo zimenezi zimandichititsa mantha.” (Salimo 139:14) Anthu ambiri amachita chidwi akaganizira mmene mwana amayambira m’mimba mwa mayi ake. Zimenezi zimawachititsa kuti aziona kuti pali winawake amene analenga zamoyo zonse.—Werengani Salimo 139:13-17; Aheberi 3:4.

Mulungu ndi amene analenga zinthu zamoyo, dziko lapansi komanso zina zonse. (Salimo 36:9) Amalankhula nafe kudzera m’Baibulo ndipo watiuza zokhudza iyeyo.—Werengani Yesaya 45:18.

Kodi anthufe tinachokera ku nyama?

Mmene thupi lathu linapangidwira limafanana kwambiri ndi thupi la nyama. Zimenezi zili choncho chifukwa Mulungu analenga anthufe komanso nyama kuti tizikhala padziko lapansi. Munthu woyambirira sanachokere ku nyama koma Mulungu anachita kumulenga kuchokera ku dothi.—Werengani Genesis 1:24; 2:7.

Koma anthu amasiyana ndi nyama m’njira ziwiri. Yoyamba, anthufe timatha kudziwa, kukonda komanso kulemekeza Mulungu. Yachiwiri, anthufe tinalengedwa kuti tisamafe pomwe nyama sanazilenge kuti zizikhala ndi moyo mpaka kalekale. Koma panopa timafa chifukwa choti tinatengera uchimo kuchokera kwa anthu awiri oyambirira, omwe sanamvere Mulungu.—Werengani Genesis 1:27; 2:15-17.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 1 m’buku lakuti, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org/ny

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena