Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 7/15 tsamba 32
  • Kodi Mukudziwa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mukudziwa?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Nkhalango
    Galamukani!—2023
  • Amosi Kodi Anali Wotchera Nkhuyu Kapena Wobaya Nkhuyu?
    Nsanja ya Olonda—2007
  • “Mbalame Zazikulu Zouluka Mogometsa”
    Galamukani!—2010
  • Munthu Aliyense Adzakhala Patsinde pa Mkuyu Wake
    Nsanja ya Olonda—2003
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 7/15 tsamba 32
Nkhalango ya Biriya ku Galileya

Nkhalango ya Biriya ku Galileya

KODI MUKUDZIWA?

Baibulo limasonyeza kuti ku Isiraeli kunali mitengo yambiri. Kodi zimenezi n’zoona?

BAIBULO limasonyeza kuti m’madera ena a Dziko Lolonjezedwa munali mitengo yambiri. (Yos. 17:15, 18; 1 Maf. 10:27) Koma masiku ano m’madera ambiri m’dzikoli mulibe mitengo. Choncho anthu ena amakayikira zimene Baibulo limanena.

Nkhuyu

Nkhuyu

Buku lina limafotokoza kuti kale ku Isiraeli kunali mitengo yambiri kuposa yomwe iliko masiku ano. M’mapiri ambiri munali mitengo ya mitundu yosiyanasiyana monga paini. Ndiponso m’dera la Sefela, lomwe lili pakati pa mapiri ndi nyanja ya Mediterranean, munali mitengo yambiri ya mkuyu.

Buku linanso limanena kuti malo ena ku Isiraeli masiku ano kulibiretu mitengo. Limafotokoza kuti mitengoyi inkatha pang’onopang’ono ndipo limati: “Anthu ndi amene awononga kwambiri mitengo pofuna kupeza malo olima, malo odyetsera ziweto, mitengo yomangira nyumba ndiponso nkhuni.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena