Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 11/1 tsamba 3
  • Kodi Mulungu Amagwirizana Ndi Zoti Anthu Azimenya Nkhondo?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mulungu Amagwirizana Ndi Zoti Anthu Azimenya Nkhondo?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Nkhondo
    Galamukani!—2017
  • Kodi Mulungu Amagwirizana Ndi Zoti Anthu Azimenya Nkhondo Masiku Ano?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhondo Yothetsa Ndhondo
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Kodi Mulungu Ankagwirizana Ndi Zoti Anthu Azimenya Nkhondo M’nthawi ya Atumwi?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 11/1 tsamba 3
Asilikali, kasinja komanso ndege zankhondo

NKHANI YA PACHIKUTO

Kodi Mulungu Amagwirizana Ndi Zoti Anthu Azimenya Nkhondo?

Kodi munthu atakufunsani funso limeneli, mungamuyankhe bwanji? Ambiri amaganiza kuti Mulungu amagwirizana ndi zoti anthu azimenya nkhondo. Amanena kuti m’Baibulo muli umboni wambirimbiri wosonyeza kuti Mulungu ankalamula anthu ake kuti azimenya nkhondo. Komabe ena amadabwa akaganizira zoti Yesu, yemwe ndi mwana wa Mulungu, analamula otsatira ake kuti azikonda adani awo. (Mateyu 5:43, 44) Chifukwa cha zimenezi amanena kuti poyamba Mulungu ankavomereza kuti anthu azimenya nkhondo, koma kenako anasintha maganizo.

Kodi inuyo mukuganiza bwanji? Kodi Mulungu amagwirizana ndi zoti anthu azimenya nkhondo? Ngati amatero, kodi amakhala mbali ya ndani pa nkhondo zomwe zimachitika masiku ano? Kudziwa mayankho a mafunsowa kungakuthandizeni kwambiri. Mwachitsanzo, tiyerekeze kuti mwadziwa zoti Mulungu amavomereza kuti anthu azimenya nkhondo ndiponso kuti ali ku mbali ya gulu limene inunso mukufuna kuti lipambane. Kodi mungaone kuti munasankha molakwika? Ayi, ndipo simungakayikire kuti gulu lanulo lipambana. Koma kodi mungamve bwanji ngati mutadziwa kuti Mulungu ali kumbali ya gulu linalo? Mwina pamenepo mungafunike kuganizanso kawiri.

Kudziwa maganizo a Mulungu pa nkhani ya nkhondo n’kofunika kwambiri chifukwa kungakuthandizeni kuti mumudziwe bwino. Ngati inuyo mukukumana ndi mavuto chifukwa cha nkhondo kapena ngati zimakupwetekani mukaona anthu akuvutika chifukwa cha nkhondo, mwina mungaganize kuti Mulungu ndi wankhanza. Kapena mungamaganize kuti sizimamukhudza n’komwe akamaona anthu akuponderezedwa.

Komatu mungadabwe kudziwa kuti zimene Baibulo limanena n’zosiyana kwambiri ndi zimene anthu amaganiza. Komanso si zoona kuti poyamba Mulungu ankagwirizana ndi zoti anthu azimenya nkhondo koma kenako anasintha maganizo. Tsopano tiyeni tione ngati Mulungu ankagwirizana ndi zoti anthu azimenya nkhondo m’nthawi ya Aisiraeli, m’nthawi ya atumwi, komanso ngati amagwirizana nazo masiku ano. Tionanso ngati nkhondo zidzathe kapena ayi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena