Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/01 tsamba 6
  • Chikondi Chimatisonkhezera Kulalikira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chikondi Chimatisonkhezera Kulalikira
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • “Chikondi Chimene Khristu Ali Nacho Chimatikakamiza”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
  • “Uzikonda Yehova Mulungu Wako”
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Utumiki Wathu—Umboni wa Chikondi Choona
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • “Pitani Mukaphunzitse Anthu a Mitundu Yonse”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 3/01 tsamba 6

Chikondi Chimatisonkhezera Kulalikira

1 Monga Mboni za Yehova timadziŵika bwino ndi kulalikira uthenga wa Ufumu mwachangu. (Mat. 24:14) Anthu oposa sikisi miliyoni padziko lonse ali pakalikiliki; chiŵerengero chimakula atsopano akayamba kulalikira nawo. Amaŵerenga okhawo amene akugwira nawo ntchitoyi.

2 Kodi n’chiyani chimatisonkhezera kudzipereka kugwira ntchito yovuta ngati imeneyi? Sitikakamizidwa, kukopeka ndi chuma chakuthupi kapena kufuna ulemu wapadera. Poyamba, ambirife tinali amantha chifukwa timadziona kuti sitikuyenera, komanso nthaŵi zambiri anthu ankatsutsa. (Mat. 24:9) Ambiri sangamvetse chimene chimatisonkhezera. Koma pali chifukwa chimene chimatisonkhezera kupitirizabe.

3 Mphamvu ya Chikondi: Yesu anatchula lamulo lalikulu koposa onse pamene anati ‘tizikonda Ambuye Mulungu wathu ndi mtima wathu wonse, ndi moyo wathu wonse, ndi nzeru zathu zonse, ndi mphamvu zathu zonse.’ (Marko 12:30) Timam’konda kwambiri Yehova chifukwa timayamikira umunthu wake ndi zochita zake—Wolamulira Wamkulu, Mlengi wa zinthu zonse woyenera “kulandira ulemerero ndi ulemu ndi mphamvu.” (Chiv. 4:11) Mikhalidwe yake yodabwitsayo n’njosayerekezeka.—Eks. 34:6, 7.

4 Kudziŵa Yehova ndi kumukonda kumatisonkhezera kuwalitsa kuunika kwathu pamaso pa anthu. (Mat. 5:16) Kuunika kwathu kumawala pamene tim’tamanda poyera, tilankhula za ntchito zake zodabwitsa, ndi pamene tifalitsa uthenga wa Ufumu wake. Mofanana ndi mngelo wouluka pakati pa mlengalenga, tili ndi ‘uthenga wabwino wosatha, tiulalikire kwa mtundu uliwonse ndi fuko ndi manenedwe ndi anthu.’ (Chiv. 14:6) Chikondi n’chimene chimatisonkhezera kugwira ntchito yolalikira yapadziko lonse.

5 Dziko limaona ntchito yathu yolalikira kukhala ‘yopusa’ yofunika kuinyalanyaza. (1 Akor. 1:18) Anthu ayesa njira zosiyanasiyana kuti athetse ntchito yathu. Chikondi chenicheni chatilimbikitsa kulengeza molimba mtima kuti: “Sitingathe ife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva. . . . Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu.” (Mac. 4:20; 5:29) Ntchito yolalikira ikupitirira kukula m’mbali zonse za dziko lapansi ngakhale pali zitsutso.

6 Kukonda kwathu Yehova kuli ngati moto wotentha umene umatisonkhezera kulalikira ponseponse zoposa zake. (Yer. 20:9; 1 Pet. 2:9) Tidzapitiriza ‘kulalikira machitidwe ake mwa mitundu ya anthu pakuti wachita zaulemerero’!—Yes. 12:4, 5.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena