CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | YOBU 16-20
Tizilimbikitsa Anzathu Powayankhula Mokoma Mtima
Munthu wopereka malangizo ayenera kuyankhula molimbikitsa kwa ena
Yobu anavutika maganizo kwambiri, choncho ankafunika kulimbikitsidwa
Anzake atatu a Yobu sananene chilichonse chomulimbikitsa. Iwo ankangomuimba mlandu ndipo zinamusokoneza maganizo kwambiri
Yobu analira chifukwa cha mawu opweteka a Bilidadi
Yobu anadandaulira Mulungu kuti amuthandize kupezako mpumulo, ngakhale kufa kumene
Yobu ankakhulupirira kwambiri kuti akufa adzauka ndipo anakhala wokhulupirika nthawi yonse yomwe anakumana ndi mavuto