Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 April tsamba 7
  • Mnzako Weniweni Amakuuza Malangizo Othandiza

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mnzako Weniweni Amakuuza Malangizo Othandiza
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Phunziro pa Kusamalira Mavuto
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira
    Bwererani kwa Yehova
  • Mphotho ya Yobu—Magwero a Chiyembekezo
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 April tsamba 7

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | YOBU 33-37

Mnzako Weniweni Amakuuza Malangizo Othandiza

Losindikizidwa

Elihu atayamba kuyankhula, ananena malangizo abwino kwambiri kusiyana ndi amene ananena Elifazi, Bilidadi ndi Zofari. Ankachitanso zinthu mokoma mtima pa nthawi imene ankayankhula ndi Yobu. Zimene anachitazi zikusonyeza kuti anali mnzake weniweni wa Yobu amene anamuthandizadi. Ndipo ife tingachite bwino kumutsanzira.

Elihu akuyankhula ndi Yobu pamene Elifazi, Bilidadi ndi Zofari akungoyang’ana

MLANGIZI WABWINO AYENERA KUKHALA:

ELIHU NDI CHITSANZO CHABWINO

32:4-7, 11, 12; 33:1

  • WOLEZA MTIMA

  • WOMVETSERA

  • WAULEMU

  • Elihu anadikira moleza mtima kuti anzake a Yobu omwe anali aakulu kwa iyeyo amalize kaye kuyankhula

  • Iye anamvetsera kaye nkhaniyo mwatcheru n’cholinga choti amupatse Yobu malangizo othandiza

  • Poyankhula ndi Yobu ankamutchula dzina lake komanso ankamuyankhula monga mnzake wapamtima

33:6, 7, 32

  • WODZICHEPETSA

  • WOCHEZEKA

  • WACHIFUNDO

  • Elihu anali wodzichepetsa komanso wokoma mtima ndipo anavomereza kuti nayenso anabadwa ndi uchimo

  • Ankamumvera chifundo Yobu chifukwa cha mavuto ake

33:24, 25; 35:2, 5

  • WOGANIZA BWINO

  • WOKOMA MTIMA

  • WOOPA MULUNGU

  • Elihu anathandiza Yobu kuzindikira kuti ankaganiza molakwika

  • Elihu anathandiza Yobu kuti asamaone ngati chinthu chofunika kwambiri ndicho kudziona ngati wolungama

  • Malangizo a Elihu anathandiza kwambiri kuti Yobu asavutike kulandira malangizo ochokera kwa Yehova

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena