Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 June tsamba 5
  • Yehova Sadzasiya Anthu Amtima Wosweka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Sadzasiya Anthu Amtima Wosweka
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Chifundo cha Yehova Chimatipulumutsa Kukugwiritsidwa Mwala
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Yehova Ndi Wofunitsitsa Kukukhululukirani
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Amakhululukira Munthu wa “Mtima Wosweka ndi Wolapa”
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Yehova Samapeputsa Mtima Wosweka
    Nsanja ya Olonda—1993
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 June tsamba 5

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MASALIMO 45-51

Yehova Sadzasiya Anthu Amtima Wosweka

Davide anayamba kuvutika mumtima atauzidwa fanizo la munthu wachuma yemwe analanda kamwana kankhosa ka munthu wosauka

Davide analemba Salimo 51 pambuyo poti mneneri Natani waulula tchimo lachigololo lomwe Davideyo anachita ndi Bateseba. Zimenezi zinkamusautsa mumtima ndipo anadzichepetsa n’kuvomereza tchimo lakelo.—2 Sam. 12:1-14.

Ngakhale kuti Davide anachimwa, Mulungu anali wokonzeka kumukhululukira

51:3, 4, 8-12, 17

  • Asanavomereze ndiponso kulapa tchimo lakelo, ankasowa mtendere

  • Davide anavutika mumtima atadziwa kuti wakhumudwitsa Mulungu, mofanana ndi mmene munthu amamvera mafupa ake akaphwanyidwa

  • Iye ankafunitsitsa kukonzanso ubwenzi wake ndi Mulungu komanso kukhululukidwa n’cholinga choti azisangalala ngati poyamba

  • Iye anapempha Yehova modzichepetsa kuti amuthandize kukhala ndi mtima womvera

  • Ankakhulupirira ndi mtima wonse kuti Yehova amukhululukira

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena