Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 July tsamba 3
  • Tamandani Yehova Wakumva Pemphero

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tamandani Yehova Wakumva Pemphero
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Mmene Mungapemphelere ndi Kumvedwa
    Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya
  • Pemphero Lingakuthandizeni Kukhala pa Ubwenzi ndi Mulungu
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Mapemphero Amene Amayankhidwa
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Kwezani Manja Okhulupirika m’Pemphero
    Nsanja ya Olonda—1999
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 July tsamba 3

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MASALIMO 60-68

Tamandani Yehova Wakumva Pemphero

Muzipempha Yehova kuti akuthandizeni kukwaniritsa zomwe munamulonjeza

61:1, 8

  • Tikamauza Yehova m’pemphero zimene tamulonjeza, zimatithandiza kuti tikwaniritsedi zimene tamulonjezazo

  • Chinthu chofunika kwambiri chimene tingalonjeze Mulungu n’choti tidzamutumikira kwa moyo wathu wonse

Hana akupemphera

Hana

Muzisonyeza kuti mumakhulupirira Yehova pomuuza zakukhosi kwanu

62:8

  • Mapemphero athu angakhale abwino kwambiri ngati titamafotokozera Yehova zimene zili mumtima mwathu

  • Tikamatchula m’pemphero chinthu chenicheni chimene tikufuna, sitivutika kuzindikira kuti Yehova wayankha mapemphero athu

Yesu akupemphera

Yesu

Yehova amamva mapemphero a anthu a mitima yabwino

65:1, 2

  • Yehova amamvetsera mapemphero a “anthu a mitundu yonse” omwe amafunitsitsa kumudziwa komanso kuchita zofuna zake

  • Tikhoza kupemphera kwa Yehova nthawi iliyonse

Koneliyo akupemphera

Koneliyo

Lembani nkhani zina zimene mukufuna kutchula m’mapemphero anu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena