Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 October tsamba 5
  • Nzeru Ndi Yabwino Kuposa Golide

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nzeru Ndi Yabwino Kuposa Golide
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • “Nzeru Itchinjiriza”
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Uchi—Mankhwala Ozuna
    Galamukani!—2002
  • ‘Wodala Munthu Wopeza Nzeru’
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Nzeru Yeniyeni Ikufuula
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 October tsamba 5

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MIYAMBO 12-16

Nzeru Ndi Yabwino Kuposa Golide

Losindikizidwa
Pasikelo pali mpukutu wolemera kuposa ndalama zachitsulo zagolide

Kodi nzeru yochokera kwa Mulungu ndi yamtengo wapatali chifukwa chiyani? Imathandiza anthu kuti asamachite zinthu zoipa komanso imateteza moyo wawo. Imawathandizanso kuti akhale ndi khalidwe labwino ndiponso kuti azilankhula zabwino.

Nzeru imathandiza munthu kuti asakhale wodzikuza

16:18, 19

  • Munthu wodzikuza

    Munthu wanzeru amazindikira kuti Yehova ndi amene amapereka nzeru

  • Anthu amene zinthu zikuwayendera bwino komanso omwe apatsidwa udindo winawake ayenera kusamala kwambiri kuti asakhale onyada kapena odzikuza

Nzeru imathandiza munthu kuti azilankhula zolimbikitsa

16:21-24

  • Munthu akulankhula ndipo wina akumvetsera

    Munthu wanzeru amayesetsa kuzindikira zinthu zabwino zimene ena amachita ndipo amalankhula zabwino zokhudza anthuwo

  • Mawu anzeru amakhala olimbikitsa ndiponso okoma ngati uchi, osati aukali kapena oyambitsa mikangano

KODI MUKUDZIWA?

Chisa cha njuchi

Uchi umagayidwa mosavuta ndipo umapatsa munthu mphamvu mwamsanga. Anthu amakonda uchi chifukwa ndi wokoma komanso umatha kugwiritsidwa ntchito monga mankhwala.

Mawu okoma amalimbikitsa munthu mofanana ndi mmene uchi umathandizira thupi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena