CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MALIRO 1-5
Mtima Wodikira Umatithandiza Kuti Tipirire
Kodi n’chiyani chinathandiza kuti Yeremiya apirire ngakhale kuti anakumana ndi mavuto aakulu?
Iye ankakhulupirira ndi mtima wonse kuti Yehova ‘adzaweramira’ anthu ake omwe analapa n’kuwapulumutsa m’mavuto awo
Iye anaphunzira ‘kunyamula goli lake ali mnyamata.’ Munthu akamapirira mayesero ali wamng’ono zimamuthandiza kuti adzathe kupirira mavuto omwe angadzakumane nawo m’tsogolo