Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 August tsamba 8
  • Muzikhala ndi Makhalidwe Amene Mulungu Amasangalala Nawo​—Chikhulupiriro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzikhala ndi Makhalidwe Amene Mulungu Amasangalala Nawo​—Chikhulupiriro
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • “Tiwonjezereni Chikhulupiriro”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Chikhulupiriro Chimatipatsa Mphamvu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Muzisonyeza Kuti Mumakhulupirira Malonjezo a Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Kodi Mumakhulupiriradi Uthenga Wabwino?
    Nsanja ya Olonda—2003
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 August tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzikhala ndi Makhalidwe Amene Mulungu Amasangalala Nawo​—Chikhulupiriro

N’CHIFUKWA CHIYANI KUKHALA NDI CHIKHULUPIRIRO N’KOFUNIKA?

  • Chikhulupiriro n’chofunika kuti tizichita zimene Mulungu amasangalala nazo.​—Aheb. 11:6

  • Kukhulupirira zimene Mulungu anatilonjeza kumatithandiza kupirira tikakumana ndi mayesero.​—1 Pet. 1:6, 7

  • Kupanda chikhulupiriro kungachititse munthu kuti achite tchimo.​—Aheb. 3:12, 13

KODI TINGASONYEZE BWANJI KUTI TILI NDI CHIKHULUPIRIRO?

  • Tizipemphera kuti tikhale ndi chikhulupiriro.​—Luka 11:9, 13; Agal. 5:22

  • Tiziwerenga Mawu a Mulungu ndi kuwasinkhasinkha.​—Aroma 10:17; 1 Tim. 4:15

  • Nthawi zonse tizicheza ndi anthu amene ali ndi chikhulupiriro.​—Aroma 1:11, 12

Banja likuphunzira maulosi a m’Baibulo okhudza zimene zichitike posachedwapa

Kodi ndingalimbitse bwanji chikhulupiriro changa komanso cha anthu a m’banja langa?

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZICHITA ZINTHU ZIMENE ZINGAKULIMBIKITSENI KUKHALA OKHULUPIRIKA​—CHIKHULUPIRIRO, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi “chikhulupiriro chopanda chinyengo” chimakhala chotani? (1 Tim. 1:5)

  • Kuti tikhale ndi chikhulupiriro cholimba, kodi tiyenera kupewa maganizo olakwika ati?

  • N’chifukwa chiyani tidzafunika kukhala ndi chikhulupiriro pa nthawi ya chisautso chachikulu? (Aheb. 10:39)

CHITSANZO CHA M’BAIBULO CHOFUNIKA KUCHIGANIZIRA:

Abulahamu anakhulupirira Yehova ngakhale pamene kuchita zimenezi kunali kovuta.​—Aheb. 11:8-10, 17-19

Dzifunseni kuti, ‘Kodi ineyo ndingatsanzire bwanji chikhulupiriro cha Abulahamu?’

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena