Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp24 No. 1 tsamba 3
  • Tonsefe Tili Ndi Udindo Wosankha Choyenera Ndi Chosayenera

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tonsefe Tili Ndi Udindo Wosankha Choyenera Ndi Chosayenera
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2024
  • Nkhani Yofanana
  • Muzikhulupirira Yehova Kuti Muzisankha Zochita Mwanzeru
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Zosankha Zanu Zizilemekeza Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2011
  • N’chiyani Chingatithandize Kuti Tizisankha Zinthu Mwanzeru?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Mawu Oyamba
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2024
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2024
wp24 No. 1 tsamba 3
Mnyamata akufunsira njira kwa mzimayi wogwira ntchito kupaki. Mzimayiyu akugwiritsa ntchito mapu pomusonyeza njira yomwe ingakamufikitse pamwamba pa phiri pomwe akufuna kupita.

Tonsefe Tili Ndi Udindo Wosankha Choyenera Ndi Chosayenera

Ngati mukufuna kupita kudera lina lomwe simunapiteko, kodi mungachite chiyani?

  1. 1. Kudzera njira yomwe mukungoiganizira.

  2. 2. Kutsatira anthu ena poganiza kuti akudziwa bwino njira ya kumene mukupita.

  3. 3. Kufufuza njira yolondola pogwiritsa ntchito mapu kapena kufunsa mnzanu wodalirika amene akudziwa bwino njira ya kumene mukufuna kupita.

Ngati tingayendere maganizo oyamba ndi achiwiriwo titha kufika kwinakwake koma osati kumene timafunadi kupita. Koma ngati tingayendere maganizo achitatuwo, n’zosakayikitsa kuti tikafika bwinobwino kumene tikufuna kupitako.

Moyo wathu uli ngati ulendo ndipo timayembekezera kuti tsogolo lathu lidzakhala losangalatsa kwambiri. Koma tingakafike kumene tikupita kapena ayi potengera kumene timafufuza malangizo otithandiza kusankha zochita.

Zinthu zambiri zimene timafunika kusankha zochita, zimakhala zing’onozing’ono pomwe zina zimakhala zofunika kwambiri. Zimene timasankha zimasonyeza mfundo za makhalidwe abwino zimene timayendera, komanso mmene timaonera zoyenera ndi zosayenera. Kwa nthawi yaitali, zimenezi zimakhudza ifeyo ndiponso anthu ena omwe timawakonda ndipo zingawabweretsere mavuto kapena ayi. Zosankha zimenezi zimakhudza nkhani monga izi:

  • Kugonana ndiponso ukwati

  • Kuchita zinthu moona mtima, ntchito ndi ndalama

  • Kulera ana

  • Mmene tingachitire zinthu ndi ena

Kodi mungatsimikizire bwanji kuti zosankha zanu pa nkhani zimenezi zidzathandiza kuti inuyo limodzi ndi banja lanu mukhale moyo wosangalala?

Aliyense ayenera kumadzifunsa funso ili: Kodi n’chiyani chimene chingandithandize kusankha zinthu mwanzeru pa nkhani zokhudza zoyenera ndi zosayenera?

Magaziniyi ifotokoza chifukwa chake Baibulo lili buku lodalirika posankha zoyenera ndi zosayenera komanso mmene lingachitire zimenezi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena