Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w25 January tsamba 32
  • Kujambula Kumathandiza Kuti Tizikumbukira Zinthu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kujambula Kumathandiza Kuti Tizikumbukira Zinthu
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Nkhani Yofanana
  • “Kuyandikira kwa Mulungu Ndi Chinthu Chabwino” kwa Ife
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • N’zotheka Ndithu Kuchepetsa Vuto la Kuiwala
    Galamukani!—2009
  • “Nthawi Zonse Iye Ankalankhula Nawo Pogwiritsa Ntchito Mafanizo”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
  • Kugwiritsa Ntchito Bwino Zinthu Zooneka
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
w25 January tsamba 32

MFUNDO ZOTHANDIZA POPHUNZIRA

Kujambula Kumathandiza Kuti Tizikumbukira Zinthu

Mwina inunso mumavutika kukumbukira zimene mwaphunzira. Koma kodi munaona kuti zimakhala zosavuta kukumbukira mafanizo a Yesu? Zili choncho chifukwa mumatha kuona m’maganizo mwanu zimene ananena ndipo zimenezi zimathandiza kuti muzizikumbukira. Muthanso kumakumbukira zimene mumawerenga ngati mumaziona m’maganizo mwanu. Kodi mungachite bwanji zimenezi? Muzijambula zithunzi pamene mukuphunzira.

Anthu amene amajambula zinthu zatsopano zimene aphunzira saziiwala. Kuchita zimenezi kumawathandiza kuti azikumbukira mawu komanso mfundo zikuluzikulu zimene aphunzira. Iwo amangojambula zinthu zosavuta osati zaluso kwambiri. Ndipo zikuoneka kuti anthu achikulire angapindule kwambiri ndi njira imeneyi.

Ulendo wina mukamadzaphunzira, mudzayese kujambula zithunzi za zimene mwaphunzirazo. Mudzadabwa kuti mudzakumbukira zinthu zambiri.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena