Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 27
  • Kodi Ndingatchule Zinthu Ziti Popemphera?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Ndingatchule Zinthu Ziti Popemphera?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Tili Ndi Mwayi Wopemphera kwa Mulungu
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kuyandikira kwa Mulungu m’Pemphero
    Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
  • Kodi Ndizipemphera Bwanji?—Kodi Ndizigwiritsa Ntchito Pemphero la Ambuye?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Pemphero Lingakuthandizeni Kuti Mulungu Akhale Mnzanu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 27

Kodi Ndingatchule Zinthu Ziti Popemphera?

Yankho la m’Baibulo

Popemphera mukhoza kutchula chinthu chilichonse chogwirizana ndi zimene Mulungu amafuna. Pa mfundo imeneyi, Baibulo limati: “Chilichonse chimene tingamupemphe [Mulungu] mogwirizana ndi chifuniro chake, amatimvera.” (1 Yohane 5:14) Kodi muyenera kutchulanso mavuto anu? Inde. Baibulo limati: “Mukhuthulireni [Mulungu] za mumtima mwanu.”—Salimo 62:8.

Zinthu zimene tingapemphe

  • Kuti tizikhulupirira kwambiri Mulungu.—Luka 17:5.

  • Kuti mzimu woyera, kapena kuti mphamvu imene Mulungu amagwiritsa ntchito, uzitithandiza kuchita zabwino.—Luka 11:13.

  • Kuti atipatse mphamvu zoti tithe kulimbana ndi mavuto athu komanso tipirire mayesero.—Afilipi 4:13.

  • Kuti atipatse mtendere wamumtima.—Afilipi 4:6, 7.

  • Kuti atipatse nzeru zotithandiza kuti tizitha kusankha bwino zochita.—Yakobo 1:5.

  • Kuti atipatse zinthu zofunikira pa moyo wa tsiku ndi tsiku.—Mateyu 6:11.

  • Kuti atikhululukire machimo athu.—Mateyu 6:12.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena