Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 54
  • N’chifukwa Chiyani Anthu Amafa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’chifukwa Chiyani Anthu Amafa?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Kodi Yesu Amapulumutsa Motani?
    Nsanja ya Olonda—2001
  • N’chifukwa chiyani Yesu Anafa?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Tchimo Loyambirira Linali Chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—1988
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 54

N’chifukwa Chiyani Anthu Amafa?

Yankho la m’Baibulo

Mwachibadwa anthufe timadabwa, makamaka wachibale wathu akamwalira, kuti n’chifukwa chiyani anthu amafa. Baibulo limanena kuti: “Mphamvu imene imabala imfa ndiyo uchimo.”—1 Akorinto 15:56.

N’chifukwa chiyani anthu onse amachimwa komanso kufa?

Adamu ndi Hava, omwe anali anthu oyambirira kulengedwa, anafa chifukwa anachimwira Mulungu. (Genesis 3:17-19) Anthu anayamba kufa chifukwa Adamu ndi Hava anakana kumvera Mulungu, yemwe ndi “kasupe wa moyo.”—Salimo 36:9; Genesis 2:17.

Adamu anapatsira uchimo ana ake onse. Baibulo limanena kuti: “Monga mmene uchimo unalowera m’dziko kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mwa uchimo, imfayo n’kufalikira kwa anthu onse chifukwa onse anachimwa.” (Aroma 5:12) Choncho anthu onse amafa chifukwa onse anachimwa.—Aroma 3:23.

Zimene Mulungu adzachite pothetsa imfa

Mulungu watilonjeza kuti “adzameza imfa kwamuyaya.” (Yesaya 25:8) Iye adzachita zimenezi pochotsa chinthu chimene chimayambitsa imfayo chomwe ndi uchimo. Mulungu adzachita zimenezi kudzera mwa Yesu Khristu, amene “akuchotsa uchimo wa dziko.”—Yohane 1:29; 1 Yohane 1:7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena