Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 58
  • Kodi Baibulo Limaletsa Kugonana?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Baibulo Limaletsa Kugonana?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Lingaliro Lanu la Kugonana—Kodi Limapanga Kusiyana Kotani?
    Mtendere Weniweni ndi Chisungiko—Kodi Mungazipeze Motani?
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Banja?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Kukhulupirika M’banja N’kutani?
    Galamukani!—2009
  • Kugonana Musanakwatirane
    Galamukani!—2013
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 58

Kodi Baibulo Limaletsa Kugonana?

Yankho la m’Baibulo

Baibulo sililetsa kugonana koma limasonyeza kuti kugonanako ndi mphatso yochokera kwa Mulungu imene anthu okwatirana ayenera kusangalala nayo. Mulungu analenga “mwamuna ndi mkazi” ndipo anaona kuti zonse zimene analenga zinali “zabwino kwambiri.” (Genesis 1:27, 31) Pa nthawi imene Mulungu ankapereka Hava kwa Adamu kuti akhale mkazi wake, ananena kuti “iwo adzakhala thupi limodzi.” (Genesis 2:24) Umenewu unali ukwati woyambirira ndipo Adamu ndi mkazi wake anafunika kumakondana kwambiri komanso kumasangalala ndi mphatso ya kugonana.

Ponena za chisangalalo chimene mwamuna wokwatira amapeza mwa mkazi wake, Baibulo limati: “Usangalale ndi mkazi wapaunyamata wako . . . Mabere ake akukhutiritse nthawi zonse. Nthawi zonse uzikhala wokondwa kwambiri ndi chikondi chake.” (Miyambo 5:18, 19) Mulungu amafunanso kuti akazi okwatiwa azisangalala kwambiri akamagonana ndi amuna awo. Baibulo limati: “Mwamuna azikhutiritsa mkazi wake pogonana nayenso mkazi azikhutiritsa mwamuna wake.”—1 Akorinto 7:3, God’s Word Bible.

Zimene Baibulo limaletsa pa nkhani yogonana

Mulungu anakonza zoti anthu okhawo amene ayenera kugonana ndi okwatirana basi. Pamfundo imeneyi, lemba la Aheberi 13:4 limati: “Ukwati ukhale wolemekezeka kwa onse, ndipo pogona pa anthu okwatirana pakhale posaipitsidwa, pakuti Mulungu adzaweruza adama ndi achigololo.” Choncho anthu okwatirana ayenera kukhala okhulupirika ndipo sayenera kugonana ndi munthu wina aliyense yemwe si mkazi kapena mwamuna wawo. Ndipotu mwamuna kapena mkazi wapabanja amakhala wosangalala kwambiri akamapewa mtima wadyera wongofuna kudzikhutiritsa, koma akamatsatira mfundo ya m’Baibulo iyi: “Kupatsa kumabweretsa chimwemwe chochuluka kuposa kulandira.”—Machitidwe 20:35.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena