7 Koma iwo anayankha kuti: “Munthuyo anachita kufunsa zokhudza ife ndi banja lathu kuti, ‘Kodi bambo anu adakali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ndipo ife tinamuuza zoona.+ Nanga tikanadziwa bwanji zoti anena kuti, ‘Mukabwere naye kuno mʼbale wanuyoʼ?”+