18 Koma amunawo atapita nawo kunyumba kwa Yosefe, anachita mantha ndipo anati: “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zimene anatibwezera mʼmatumba athu pa ulendo woyamba uja. Anthu amenewa atiukira nʼkutigwira kuti tikhale akapolo ndipo atilanda abulu athu!”+