14 Poyankha iye anati: “Ndi ndani anakupatsa udindo woti uzitilamulira komanso kutiweruza? Kodi ukufuna kundipha ngati mmene unaphera nzika ya mu Iguputo ija?”+ Zitatero Mose anachita mantha ndipo mumtima mwake anati: “Apa nkhani ija yadziwika basi!”