18 Nsalu yotchinga pakhomo la bwalo anaiwomba ndi ulusi wabuluu, ubweya wa nkhosa wapepo, ulusi wofiira kwambiri ndi ulusi wopota wabwino kwambiri. Inali mamita 9 mulitali mwake, ndipo kutalika kwake kuchokera pansi mpaka mʼmwamba inali mamita awiri, mofanana ndi nsalu zotchingira mpanda wa bwalo.+