16 Eleazara+ mwana wa wansembe Aroni ndi amene ali ndi udindo woyangʼanira mafuta a nyale,+ zofukiza zonunkhira,+ nsembe ya nthawi zonse yambewu ndi mafuta odzozera.+ Ali ndi udindo woyangʼanira chihema chonse ndi zinthu zonse za mmenemo, kuphatikizapo malo oyera ndi ziwiya zake.”