29 Chifukwa ndikudziwa bwino kuti pambuyo pa imfa yanga, mosakayikira mudzachita zinthu zoipa+ nʼkupatuka kusiya njira imene ndakulamulani. Ndiyeno pamapeto pake tsoka lidzakugwerani,+ chifukwa mudzachita zoipa pamaso pa Yehova ndipo mudzamukhumudwitsa ndi ntchito za manja anu.”