8 Yehova anapereka adaniwo mʼmanja mwa Aisiraeli.+ Choncho anayamba kuwagonjetsa ndipo anawathamangitsa mpaka kukafika kumzinda waukulu wa Sidoni,+ ku Misirepotu-maimu+ ndi kuchigwa cha Mizipe kumʼmawa. Anapitiriza kuwapha moti panalibe amene anapulumuka.+