-
Oweruza 4:21Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
21 Ndiyeno Yaeli mkazi wa Hiberi anatenga chikhomo cha tenti ndi hamala. Kenako analowa mutentimo, akuyenda monyangʼama.* Apa nʼkuti Sisera ali mʼtulo tofa nato chifukwa anali atatopa kwambiri. Yaeli anakhoma chikhomocho mʼmutu mwa Sisera pafupi ndi khutu. Chikhomocho chinalowa mpaka kufika pansi ndipo anafera pompo.+
-