19 Ndiyeno mzimu wa Yehova unamupatsa mphamvu.+ Choncho anapita ku Asikeloni+ nʼkukapha amuna 30 akumeneko, ndipo anatenga zovala zawo nʼkuzipereka kwa anthu amene anamasulira mwambi aja.+ Iye anali wokwiya kwambiri pamene ankabwerera kunyumba ya bambo ake.