2 Anthu a fuko la Dani anatumiza amuna 5 a mʼbanja lawo, amuna olimba mtima ochokera ku Zora ndi ku Esitaoli+ kuti akafufuze zokhudza malowo. Anawauza kuti: “Pitani mukafufuze zokhudza malowo.” Atafika kudera lamapiri la Efuraimu, kunyumba ya Mika,+ anagona kumeneko.