11 Kenako Samueli anafunsa Jese kuti: “Kodi anyamata anu onse ndi omwewa basi?” Iye anayankha kuti: “Wamngʼono kwambiri+ wachokapo. Wapita koweta nkhosa.”+ Zitatero Samueli anauza Jese kuti: “Tumizani munthu akamutenge, chifukwa sitikhala pansi kuti tidye mpaka iye atabwera.”