51 Choncho Mfumu Solomo anamaliza ntchito yonse yokhudza nyumba ya Yehova imene anayenera kugwira. Kenako Solomo anabweretsa zinthu zimene bambo ake Davide anaziyeretsa.+ Anatenga siliva, golide ndiponso zinthu zina nʼkuziika mosungira chuma chapanyumba ya Yehova.+