13 Nayonso Mfumu Solomo inapatsa mfumukazi ya ku Sheba chilichonse chimene inkafuna komanso chimene inapempha, kuwonjezera pa zimene Mfumu Solomo inamʼpatsa chifukwa cha kuwolowa manja kwake. Kenako mfumukaziyo inanyamuka nʼkumapita kwawo limodzi ndi antchito ake.+