12 Kenako Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumu+ uja nʼkumuveka chipewa chachifumu nʼkuika mpukutu wa Chilamulo cha Mulungu pamutu pake.+ Choncho anamuveka ufumu nʼkumudzoza. Ndiyeno anayamba kuwomba mʼmanja nʼkumanena kuti: “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”+