15 Koma wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a magulu a asilikali 100,+ omwe anasankhidwa kuti aziyangʼanira asilikali, ndipo anawauza kuti: “Mʼchotseni pakati pa asilikali ndipo aliyense amene angamutsatire aphedwe ndi lupanga!” Wansembeyo anali atanena kuti: “Musamuphere mʼnyumba ya Yehova.”