21 Atakambirana ndi anthuwo, iye anasankha anthu oti aziimbira+ Yehova ndiponso kumutamanda atavala zovala zokongola ndi zopatulika ndipo ankayenda patsogolo pa amuna onyamula zida. Iwo ankanena kuti: “Yamikani Yehova, chifukwa chikondi chake chokhulupirika chidzakhalapo mpaka kalekale.”+