7 Iye anaika mʼnyumba ya Mulungu woona+ chifaniziro chimene anapanga. Koma ponena za nyumba imeneyo, Mulungu anauza Davide ndi mwana wake Solomo kuti: “Mʼnyumba iyi ndiponso mu Yerusalemu mzinda umene ndausankha pa mafuko onse a Isiraeli, ndidzaikamo dzina langa mpaka kalekale.+