25 Palali mwana wa Uzai, anakonza mpandawo kutsogolo kwa khoma lothandizira kuti mpanda usagwe. Anakonzanso nsanja yochokera pa Nyumba ya Mfumu+ imene ili kumtunda mʼBwalo la Alonda.+ Pedaya mwana wa Parosi, anapitiriza kuchokera pamene Palali+ analekezera.